Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
96 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;
Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,
ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,
koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,
mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;
bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;
njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”
Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;
Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;
nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 idzayimba pamaso pa Yehova,
pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo
ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;
fuwula mokweza, iwe Israeli!
Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Yehova wachotsa chilango chako,
wabweza mdani wako.
Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;
sudzaopanso chilichonse.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,
“Usaope, iwe Ziyoni;
usafowoke.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako,
ali ndi mphamvu yopulumutsa.
Adzakondwera kwambiri mwa iwe,
adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,
adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 “Ndidzakuchotserani zowawa
za pa zikondwerero zoyikika;
nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi
onse amene anakuponderezani;
ndidzapulumutsa olumala
ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.
Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu
mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;
pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.
Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu
pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi
pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu
inu mukuona,”
akutero Yehova.
11 Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira. 12 Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika. 13 Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje. 14 Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.