Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
126 Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,
tinali ngati amene akulota.
2 Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;
malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.
Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,
“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 Yehova watichitira zinthu zazikulu,
ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,
monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Iwo amene amafesa akulira,
adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Iye amene amayendayenda nalira,
atanyamula mbewu yokafesa,
adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,
atanyamula mitolo yake.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;
Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.
Muzichitenso masiku athu ano,
masiku athu ano zidziwike;
mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,
Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.
Sela
Ulemerero wake unaphimba mlengalenga
ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;
kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,
mʼmene anabisamo mphamvu zake.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri;
nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;
anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.
Mapiri okhazikika anagumuka
ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.
Njira zake ndi zachikhalire.
Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro
12 Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.
Kutsanzira Paulo
15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.