Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Asafu.
79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;
ayipitsa Nyumba yanu yoyera,
asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu
kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,
matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 Akhetsa magazi monga madzi
kuzungulira Yerusalemu yense,
ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,
choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?
Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina
amene sakudziwani Inu,
pa maufumu
amene sayitana pa dzina lanu;
7 pakuti iwo ameza Yakobo
ndi kuwononga dziko lawo.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu
chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,
pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;
tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu
chifukwa cha dzina lanu.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti,
“Ali kuti Mulungu wawo?”
Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina
kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu;
ndi mphamvu ya dzanja lanu
muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri
kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu,
tidzakutamandani kwamuyaya,
kuchokera mʼbado ndi mʼbado
tidzafotokoza za matamando anu.
Cholinga cha Yehova
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti,
“ndidzasonkhanitsa olumala;
ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa
ndiponso amene ndinawalanga.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.
Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.
Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova
kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,
iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,
ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;
ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,
kodi ulibe mfumu?
Kodi phungu wako wawonongedwa,
kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,
ngati mayi pa nthawi yake yobereka,
pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda
ndi kugona kunja kwa mzindawo.
Udzapita ku Babuloni;
kumeneko udzapulumutsidwa,
kumeneko Yehova adzakuwombola
mʼmanja mwa adani ako.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu
yasonkhana kulimbana nawe.
Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,
maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
12 Koma iwo sakudziwa
maganizo a Yehova;
iwo sakuzindikira cholinga chake,
Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,
pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;
ndidzakupatsa ziboda zamkuwa
ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”
Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,
chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Kugwa kwa Babuloni
18 Zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika kuchokera kumwamba. Iye anali ndi ulamuliro waukulu, ndipo dziko lapansi linawala ndi ulemerero. 2 Mngeloyo anafuwula ndi mawu amphamvu kuti:
“ ‘Wagwa! Wagwa Babuloni Wamkulu!’
Wasandulika mokhalamo ziwanda
ndi kofikako mizimu yonse yoyipa
ndi mbalame zonse zonyansa
ndi zodetsedwa.
3 Pakuti mayiko onse amwa
vinyo ozunguza mutu wazigololo zake.
Mafumu a dziko lapansi achita naye chigololo,
ndipo amalonda a dziko lapansi analemera kuchokera pa zolakalaka zake zosefukira.”
Awachenjeza kuti Athawe Chiweruzo cha Babuloni
4 Ndiponso ndinamva mawu ena kuchokera kumwamba akuti:
“ ‘Anthu anga tulukani, mwa iye,’
mungachimwe naye
kuti musadzalandire nawo gawo lililonse la miliri yake;
5 pakuti machimo ake awunjikana mpaka kumwamba,
ndipo Mulungu wakumbukira milandu yake.
6 Bwezerani Iye monga momwe iye anakuchitirani.
Mubwezereni mowirikiza pa zimene anachita.
Mumusakanizire magawo awiri kuchokera mʼchikho chake.
7 Mumuzunze, kumumvetsa chisoni kwambiri
monga mwaulemerero ndi zolakalaka
zimene anadzaza mu mtima mwake. Iye anadzikuza nʼkumati,
‘Ndinakhala monga mfumu yayikazi,
ine sindine wamasiye
ndipo sindidzalira maliro.’
8 Chifukwa chake miliri yake idzamugonjetsa tsiku limodzi;
imfa, kulira maliro ndi njala.
Iye adzanyeka ndi moto
pakuti wamphamvu ndi Mulungu Ambuye amene wamuweruza.
Tsoka la Babuloni
9 “Mafumu a dziko lapansi, amene anachita naye chigololo nachita naye pamodzi zosangalatsa moyo uno, akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzalira nakhuza maliro ake. 10 Iwo adzayima kutali nalira chifukwa choopsedwa ndi mazunzo ake.
“ ‘Tsoka! Tsoka mzinda waukulu
iwe, Babuloni mzinda wamphamvu!
Mu ora limodzi chiwonongeko chako chafika!’
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.