Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 28

Salimo la Davide.

28 Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;
    musakhale osamva kwa ine.
Pakuti mukapitirira kukhala chete,
    ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Imvani kupempha chifundo kwanga
    pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,
pomwe ndikukweza manja anga
    kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,
    pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,
amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo
    koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo
    ndi ntchito zawo zoyipa;
abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita
    ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,
    ndi zimene manja ake anazichita,
Iye adzawakhadzula
    ndipo sadzawathandizanso.

Matamando apite kwa Yehova,
    popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;
    mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.
Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe
    ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,
    linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;
    mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Numeri 27:15-23

15 Mose anati kwa Yehova, 16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti 17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”

18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako. 19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona. 20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera. 21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”

22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse. 23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.

2 Timoteyo 2:8-13

Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo. 10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha.

11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa:

Ngati ife tinafa naye pamodzi,
    tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
12 Ngati tinapirira,
    tidzalamuliranso naye pamodzi.
Ngati ife timukana,
    Iye adzatikananso.
13 Ngati ndife osakhulupirika,
    Iye adzakhalabe wokhulupirika
    popeza sangathe kudzikana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.