Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
123 Ndikweza maso anga kwa Inu,
kwa Inu amene mumakhala kumwamba.
2 Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,
monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,
choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,
mpaka atichitire chifundo.
3 Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,
pakuti tapirira chitonzo chachikulu.
4 Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,
chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.
Nyimbo ya Debora
5 “Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
2 “Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;
ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,
tamandani Yehova:
3 “Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!
Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,
Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
4 “Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,
pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,
dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka
nigwetsa madzi.
5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,
Mulungu wa Israeli.
6 “Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,
pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;
alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
7 Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi
mpaka pamene iwe Debora unafika;
unafika ngati mayi ku Israeli.
8 Pamene anasankha milungu ina,
nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,
ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke
pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
9 Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,
uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.
Tamandani Yehova!
10 “Inu okwera pa abulu oyera,
okhala pa zishalo,
ndi inu oyenda pa msewu,
yankhulani. 11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;
kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;
akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.
“Choncho anthu a Yehova
anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;
tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.
Iwe Baraki! nyamuka
Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
Za Mzimu Woyipa
43 “Pamene mzimu woyipa utuluka mwa munthu, umadutsa malo wopanda madzi kufunafuna malo opumulira ndipo suwapeza. 44 Pamenepo umati, ‘Ndidzabwerera ku nyumba yanga komwe ndinatuluka.’ Pamene ufika, upeza mopanda kanthu, mosesedwa ndi mokonzedwa bwino. 45 Kenaka umapita kukatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa uwowo ndipo imapita ndi kukakhala mʼmenemo. Choncho khalidwe lotsiriza la munthu uyu limakhala loyipa kwambiri kuposa loyambalo. Umo ndi mmene zidzakhalire ndi mʼbado oyipawu.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.