Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LACHINAYI
Masalimo 90–106
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.
90 Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo
pa mibado yonse.
2 Mapiri asanabadwe,
musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,
kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi,
mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu
zili ngati tsiku limene lapita
kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,
iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,
pofika madzulo wauma ndi kufota.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,
kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,
kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,
kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;
tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;
inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
32 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;
imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula
ndipo mawu anga atsike ngati mame,
ngati mvumbi pa udzu watsopano,
ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova.
Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,
njira zake zonse ndi zolungama.
Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,
Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,
iwo si ana akenso,
koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere,
inu anthu opusa ndi opanda nzeru?
Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,
amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Kumbukirani masiku amakedzana;
ganizirani za mibado yakalekale.
Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,
akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,
pamene analekanitsa anthu onse,
anayikira malire anthu onse
molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,
Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Anamupeza mʼchipululu,
ku malo owuma ndi kopanda kanthu.
Anamuteteza ndi kumusamalira;
anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake
nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,
chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo
ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera;
popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko
ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.
Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,
ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,
ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,
pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani
ndiponso tirigu wabwino kwambiri.
Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;
munayiwala Mulungu amene anakubalani.
7 Pa zonse iwe mwini ukhale chitsanzo pa ntchito zabwino. Pa chiphunzitso chako uwonetsa kuona mtima ndi kutsimikiza mtima kwako. 8 Phunzitsa choonadi kuti anthu asapeze chokutsutsa, motero wotsutsana nawe adzachita manyazi chifukwa adzasowa kanthu koyipa kuti atinenere.
11 Pakuti chisomo cha Mulungu chimene chimapulumutsa chaonekera kwa anthu onse. 12 Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, 13 pamene tikudikira chiyembekezo chodala; kuonekera kwa ulemerero wa Mulungu wathu wamkulu ndi Mpulumutsi, Yesu Khristu, 14 amene anadzipereka yekha chifukwa cha ife kutiwombola ku zoyipa zonse ndi kudziyeretsera yekha anthu amene ndi akeake, achangu pa ntchito yabwino.
15 Tsono zimenezi ndi zinthu zomwe uyenera kuphunzitsa. Uziwalimbikitsa anthu ndi kuwatsutsa komwe. Uzichita zimenezi ndi ulamuliro wonse. Wina aliyense asakupeputse ayi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.