Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
97 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale;
magombe akutali akondwere.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira;
chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Moto umapita patsogolo pake
ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse;
dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova,
pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake,
ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi,
iwo amene amanyadira mafano;
mulambireni, inu milungu yonse!
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera,
midzi ya Yuda ikusangalala
chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi;
ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa
pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira
ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama,
ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama
ndipo tamandani dzina lake loyera.
33 Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ 2 Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. 3 Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
4 Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera. 5 Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.” 6 Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.
Kutsanzira Paulo
15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.
17 Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18 Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19 Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20 Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21 Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.
4 Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.