Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 17:1-7

Pemphero la Davide.

17 Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;
    mverani kulira kwanga.
Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa
    popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;
    maso anu aone chimene ndi cholungama.

Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,
    ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;
    Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Kunena za ntchito za anthu,
    monga mwa mawu a pakamwa panu,
Ine ndadzisunga ndekha
    posatsata njira zachiwawa.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;
    mapazi anga sanaterereke.

Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;
    tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,
    Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja
    iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.

Masalimo 17:15

15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;
    pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Yesaya 43:1-7

Yehova Yekha Mpulumutsi wa Israeli

43 Koma tsopano, Yehova
    amene anakulenga, iwe Yakobo,
    amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,
“Usaope, pakuti ndakuwombola;
    Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Pamene ukuwoloka nyanja,
    ndidzakhala nawe;
ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,
    sidzakukokolola.
Pamene ukudutsa pa moto,
    sudzapsa;
    lawi la moto silidzakutentha.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,
    Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.
Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,
    ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga,
    ndipo chifukwa ndimakukonda,
ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe,
    ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe;
    ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa,
    ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’
    ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’
Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali,
    ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
onsewo amadziwika ndi dzina langa;
    ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga,
    ndinawawumba, inde ndinawapanga.”

Mateyu 15:32-39

32 Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”

33 Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”

34 Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?”

Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”

35 Iye anawuza gululo kuti likhale pansi. 36 Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo. 37 Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri. 38 Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana. 39 Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.