Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

142 Ndikulirira Yehova mofuwula;
    ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
    ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
    ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
    anthu anditchera msampha mobisa.
Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
    palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
    palibe amene amasamala za moyo wanga.

Ndilirira Inu Yehova;
    ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
    gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
Mverani kulira kwanga
    pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
    pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
Tulutseni mʼndende yanga
    kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira
    chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Obadiya 15-21

15 “Tsiku la Yehova layandikira
    limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;
    zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera,
    koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;
iwo adzamwa ndi kudzandira
    ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;
    phirilo lidzakhala lopatulika,
ndipo nyumba ya Yakobo
    idzalandira cholowa chake.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto
    ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;
nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,
    ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.
Sipadzakhala anthu opulumuka
    kuchokera mʼnyumba ya Esau.”
            Yehova wayankhula.

19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala
    ku mapiri a Esau,
ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri
    adzatenga dziko la Afilisti.
Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,
    ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo
    adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;
a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi
    adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni
    ndipo adzalamulira mapiri a Esau.
    Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

Mateyu 13:10-17

10 Ophunzira anabwera kwa Iye ndikumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani Inu mukuyankhula kwa anthu mʼmafanizo?”

11 Iye anayankha kuti, “Nzeru zakudziwa zinsinsi za ufumu wakumwamba zapatsidwa kwa inu koma osati kwa iwo. 12 Aliyense amene ali nazo adzapatsidwa zowonjezera ndipo iye adzakhala nazo zambiri. Aliyense amene alibe, ngakhale zimene ali nazo adzamulanda. 13 Ichi ndi chifukwa chake ndimayankhula kwa iwo mʼmafanizo:

“Ngakhale akupenya koma saona,
    ngakhale akumva koma samvetsetsa kapena kuzindikira.

14 Mwa iwo zimene ananenera Yesaya zikwaniritsidwa:

“ ‘Kumva mudzamva koma osamvetsetsa.
    Kupenya mudzapenya koma osaona kanthu.
15 Pakuti mtima wa anthu awa ndi wokanika,
    mʼmakutu mwawo ndi mogontha,
    ndipo atsinzina
kuti asaone kanthu.
    Mwina angapenye ndi maso awo,
    angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka,
Ineyo nʼkuwachiritsa.’

16 Koma maso anu ndi odala chifukwa amapenya ndi makutu anu chifukwa amamva. 17 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama anafuna kuona zimene inu mukupenya koma sanazione ndi kumva zimene inu mukumva koma sanazimve.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.