Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.
142 Ndikulirira Yehova mofuwula;
ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
2 Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
3 Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
anthu anditchera msampha mobisa.
4 Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
palibe amene amasamala za moyo wanga.
5 Ndilirira Inu Yehova;
ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
6 Mverani kulira kwanga
pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
7 Tulutseni mʼndende yanga
kuti nditamande dzina lanu.
Ndipo anthu olungama adzandizungulira
chifukwa cha zabwino zanu pa ine.
1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,
mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,
pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,
Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;
Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake,
ndipo zigwa zikugawikana
ngati phula pa moto,
ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,
chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.
Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?
Kodi si Samariya?
Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?
Kodi si Yerusalemu?
Moyo Wokondweretsa Mulungu
4 Potsiriza, abale, tinakulangizani kale momwe mukuyenera kukhalira kuti mukondweretse Mulungu, monga momwe mukukhaliramo. Tsopano tikukupemphani ndi kukulimbikitsani mwa Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale. 2 Inu mukudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa ulamuliro wa Ambuye Yesu.
3 Ndi chifuniro cha Mulungu kuti muyeretsedwe: kuti mupewe dama; 4 aliyense wa inu aphunzire kulamulira thupi lake mʼnjira yoyera ndi yaulemu, 5 osati yotsata chilakolako chonyansa monga amachitira akunja, amene sadziwa Mulungu. 6 Pa zimenezi munthu asachimwire mʼbale wake kapena kumuonerera. Ambuye adzalanga anthu onse amene amachita machimo amenewa, monga tinakuwuzani kale ndi kukuchenjezani. 7 Pakuti Mulungu sanatiyitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima. 8 Choncho, aliyense amene akukana malangizo awa sakukana munthu koma Mulungu, Mulungu weniweniyo amene amakupatsani Mzimu Woyera.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.