Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 16

Mikitamu ya Davide.

16 Ndisungeni Inu Mulungu,
    pakuti ine ndimathawira kwa Inu.

Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;
    popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,
    amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina
    mavuto awo adzachulukadi.
Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi
    kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.

Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;
    mwateteza kolimba gawo langa.
Malire a malo anga akhala pabwino;
    ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.

Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;
    ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.
    Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,
    sindidzagwedezeka.

Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;
    thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,
    simudzalola kuti woyera wanu avunde.
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;
    mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,
    ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

Nyimbo ya Solomoni 5:9-6:3

Abwenzi

Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
    kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?
Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani
    kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10 Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi
    pakati pa anthu 1,000.
11 Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;
    tsitsi lake ndi lopotanapotana,
    ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 Maso ake ali ngati nkhunda
    mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,
    zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya
    zopatsa fungo lokoma.
Milomo yake ili ngati maluwa okongola
    amene akuchucha mure.
14 Manja ake ali ngati ndodo zagolide
    zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.
Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu
    woyikamo miyala ya safiro.
15 Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,
    yokhazikika pa maziko a golide.
Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,
    abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;
    munthuyo ndi wokongola kwambiri!
Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,
    inu akazi a ku Yerusalemu.

Abwenzi

Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
    kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?
Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti
    kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,
    ku timinda ta zokometsera zakudya,
akukadyetsa ziweto zake ku minda,
    ndiponso akuthyola maluwa okongola.
Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;
    amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

1 Akorinto 15:1-11

Za Kuuka kwa Khristu

15 Tsono abale, ndikufuna ndikukumbutseni za Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani. Munawulandira ndipo munawukhulupirira kolimba. Inu munapulumutsidwa ndi Uthenga Wabwinowu, ngati mwasunga mawu amene ndinakulalikirani. Kupanda kutero, mwangokhulupirira pachabe.

Pakuti chimene ndinalandira ndinapereka kwa inu monga chofunika kuposa zonse, kuti Khristu anafera zoyipa zathu monga mwa Malemba, kuti anayikidwa mʼmanda, kuti anaukitsidwa tsiku lachitatu monga mwa Malemba; ndipo kuti anaonekera kwa Petro, ndipo kenaka kwa Atumwi khumi ndi awiriwo. Pambuyo pake, Iye anaonekera kwa anthu oposa 500 mwa abale pa nthawi imodzi, ndipo ambiri mwa iwo akanali ndi moyo ngakhale kuti ena anagona tulo. Kenaka anaonekeranso kwa Yakobo, kenaka kwa atumwi onse. Potsiriza pa onse anaonekeranso kwa ine, monga mwana wobadwa nthawi isanakwane.

Pakuti ine ndine wamngʼono kwa atumwi ndipo sindiyenera nʼkomwe kutchedwa mtumwi chifukwa ndinazunza mpingo wa Mulungu. 10 Koma mwachisomo cha Mulungu, ndili mmene ndililimu, ndipo chisomo chake kwa ine sichinali chopanda ntchito. Ndinagwira ntchito kuposa ena onse a iwo. Choncho sindine koma chisomo cha Mulungu chimene chinali ndi ine. 11 Tsono kaya ndi ineyo kapena iwowo, izi ndi zomwe timalalikira, ndipo izi ndi zimene munakhulupirira.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.