Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
146 Tamandani Yehova.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;
ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Musamadalire mafumu,
anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;
zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi
Mulungu wa Yakobo.
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,
nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;
Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa
ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.
Yehova amamasula amʼndende,
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona,
Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,
Yehova amakonda anthu olungama.
9 Yehova amasamalira alendo
ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,
koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,
Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.
Tamandani Yehova.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,
ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.
Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa
ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.
Olamulira ako adzakhala a mtendere.
Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,
bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,
ndidzakhala malinga ako okuteteza
ndipo udzanditamanda.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,
kapena mwezi kuti uwunikire usiku,
pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,
ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Dzuwa lako silidzalowanso,
ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;
Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,
ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama
ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.
Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,
ntchito ya manja anga,
kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,
kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.
Ine ndine Yehova,
nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Yesu Achiritsa Osaona ndi Osayankhula
27 Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”
28 Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?”
Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”
29 Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.” 30 Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.” 31 Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.
32 Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula. 33 Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”
34 Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.