Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 81

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.

81 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
    Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Yambani nyimbo, imbani tambolini
    imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.

Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano,
    ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
ili ndi lamulo kwa Israeli,
    langizo la Mulungu wa Yakobo.
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe
    pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto,
    kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.

Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo;
    Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani,
    ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu;
    ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba.
            Sela

“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani
    ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu;
    musadzagwadire mulungu wina.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.
    Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.

11 “Koma anthu anga sanandimvere;
    Israeli sanandigonjere.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
    kuti atsate zimene ankafuna.

13 “Anthu anga akanangondimvera,
    Israeli akanatsatira njira zanga,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
    ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
    ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;
    ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

Yeremiya 2:4-13

Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo,
    inu mafuko onse a Israeli.

Yehova akuti,

“Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji,
    kuti andithawe?
Iwo anatsata milungu yachabechabe,
    nawonso nʼkusanduka achabechabe.
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti,
    amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto
natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma
    ndi lokumbikakumbika,
mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima,
    dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde
    kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.
Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa
    ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
Ansembe nawonso sanafunse kuti,
    ‘Yehova ali kuti?’
Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe;
    atsogoleri anandiwukira.
Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala,
    ndi kutsatira mafano achabechabe.

“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,”
            akutero Yehova.
    “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone,
    tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino;
    ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake?
    (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe).
Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero
    ndi mafano achabechabe.
12 Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi,
    ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,”
            akutero Yehova.
13 “Popeza anthu anga achita machimo awiri:
Andisiya Ine
    kasupe wa madzi a moyo,
ndi kukadzikumbira zitsime zawo,
    zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.

Yohane 7:14-31

Yesu Aphunzitsa pa Phwando

14 Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa. 15 Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”

16 Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma. 17 Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha. 18 Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse. 19 Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”

20 Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”

21 Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa. 22 Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata. 23 Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata? 24 Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”

Kodi Yesu ndi Khristu?

25 Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu? 26 Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu? 27 Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”

28 Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa, 29 koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”

30 Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike. 31 Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”

Yohane 7:37-39

Mitsinje ya Madzi Opatsa Moyo

37 Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe. 38 Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’ ” 39 Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.