Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
95 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,
tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko
ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,
mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,
ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,
ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,
tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu
ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,
ndi nkhosa za mʼdzanja lake.
Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,
monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,
ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;
ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera
ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,
“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
27 Komabe anthu ena anapita kuti akatole chakudya tsiku lachisanu ndi chiwiri, koma sanapeze kanthu. 28 Ndipo Yehova anafunsa Mose nati, “Kodi inu muzipitirira kukana kusunga malamulo ndi malangizo anga mpaka liti? 29 Taonani, popeza Yehova wakupatsani Sabata nʼchifukwa chake tsiku lachisanu ndi chimodzi amakupatsani chakudya cha masiku awiri. Aliyense azikhala pamene ali pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, pasapezeke wotuluka kunja.” 30 Kotero anthu anapuma tsiku lachisanu ndi chiwiri.
31 Aisraeli anatchula chakudyacho Mana. Chakudyacho chinkaoneka ngati mbewu zamapira, zoyera. Ndipo chinkakoma ngati chothira uchi. 32 Mose anati, “Chimene Yehova walamula ndi ichi: ‘Tengani muyeso wa malita awiri a mana ndi kusungira mibado imene ikubwera, kuti iwo adzaone chakudya chimene Ine ndinakupatsani kuti mudye mʼchipululu pamene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.’ ”
33 Choncho Mose anati kwa Aaroni, “Tenga mtsuko ndipo uyikemo malita awiri a mana. Ndipo uyike manawo pamaso pa Yehova kusungira mibado imene ikubwera.”
34 Monga momwe Yehova analamulira Mose, Aaroni anayika mtsuko uja pafupi ndi bokosi la Chipangano kuti manawo asungike. 35 Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani.
Yesu Acheza ndi Mayi wa ku Samariya
4 Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane, 2 (ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake). 3 Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.
4 Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya. 5 Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe. 6 Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.