Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.
51 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,
molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
molingana ndi chifundo chanu chachikulu
mufafanize mphulupulu zanga.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse
ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,
ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa
ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,
Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama
pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,
wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;
mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,
munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,
mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Mufulatire machimo anga
ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu
ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Musandichotse pamaso panu
kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu
ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu
kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,
Mulungu wa chipulumutso changa,
ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,
ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.
Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;
mtima wosweka ndi wachisoni
Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;
mumange makoma a Yerusalemu.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,
nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;
ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Kusala Kwenikweni
58 “Fuwula kwambiri, usaleke.
Mawu ako amveke ngati lipenga.
Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;
uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;
amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,
kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola
ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.
Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo
ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala
kudya pamene Inu simukulabadirapo?
Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa
pamene Inu simunasamalepo?’ ”
Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,
ndipo mumazunza antchito anu onse.
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,
mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.
Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,
kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?
Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango
ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?
Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,
tsiku lokondweretsa Yehova?
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:
Kumasula maunyolo ozunzizira anthu
ndi kumasula zingwe za goli,
kupereka ufulu kwa oponderezedwa
ndi kuphwanya goli lililonse?
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?
Osowa ndi ongoyendayenda,
kodi mwawapatsa malo ogona?
Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,
ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;
chilungamo chanu chidzakutsogolerani
ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;
mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.
“Ngati muleka kuzunza anzanu,
ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,
ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,
pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,
ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;
adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa
ndipo adzalimbitsa matupi anu.
Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,
ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,
ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;
inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.
Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
Wamkulu mu Ufumu Wakumwamba
18 Pa nthawi imeneyo ophunzira anabwera kwa Yesu ndipo anamufunsa kuti, “Wamkulu woposa onse ndani mu ufumu wakumwamba?”
2 Iye anayitana kamwana kakangʼono ndi kukayimiritsa pakati pawo. 3 Ndipo Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati simusintha ndi kukhala ngati tiana tatingʼono, simudzalowa konse mu ufumu wakumwamba. 4 Chifukwa chake, aliyense amene adzichepetsa yekha ngati kamwana aka, ameneyo ndiye wamkulu koposa onse mu ufumu wakumwamba. 5 Ndipo aliyense amene alandira kamwana kakangʼono ngati aka mu dzina langa, alandira Ine.
Za Kuchimwitsa Ena
6 “Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja. 7 Tsoka dziko lapansi chifukwa cha zinthu zimene ziyenera kubwera, koma tsoka kwa munthu amene abweretsa zotere!
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.