Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Heti
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa;
ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Ndinalingalira za njira zanga
ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
kumvera malamulo anu.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
phunzitseni malamulo anu.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera
ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide
kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola
kwa anthu amene amutuma;
iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka
ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,
ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,
kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako
ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama,
ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,
kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni
kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira
kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;
ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,
ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
Chikondi
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20 Koma,
“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.
Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.
Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.