Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
112 Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Tsoka kwa Mzinda wa Davide
29 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,
mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!
Papite chaka chimodzi kapena ziwiri
ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli
ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,
mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;
ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo
ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,
mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,
adzamveka ngati a mzukwa.
Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.
Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.
Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera
ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,
kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli
nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,
chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,
gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,
koma podzuka ali nayobe njala;
kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,
koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.
Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse
chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.
Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,
ledzerani, koma osati ndi vinyo,
dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.
Watseka maso anu, inu aneneri;
waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
Mitundu Iwiri ya Nzeru
13 Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14 Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15 “Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16 Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.
17 Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18 Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.