Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide.
37 Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa
kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga,
ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;
khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova
ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Pereka njira yako kwa Yehova;
dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,
chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;
usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo,
pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,
usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,
koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso;
ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko
ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama
ndipo amawakukutira mano;
13 koma Ambuye amaseka oyipa
pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Oyipa amasolola lupanga
ndi kupinda uta
kugwetsa osauka ndi osowa,
kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,
ndipo mauta awo anathyoka.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo
ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,
koma Yehova amasunga olungama.
Rute ndi Bowazi ku Malo Wopunthira Tirigu ndi Barele
3 Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino? 2 Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira. 3 Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa. 4 Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka. 11 Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino. 12 Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine. 13 Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
Makolo a Davide
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli. 15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi:
Perezi anali abambo a Hezironi.
19 Hezironi anali abambo a Ramu,
Ramu anali abambo a Aminadabu,
20 Aminadabu abambo a Naasoni,
Naasoni anali abambo a Salimoni,
21 Salimoni abambo a Bowazi,
Bowazi abambo a Obedi.
22 Obedi anali abambo a Yese,
ndipo Yese anali abambo a Davide.
Madalitso ndi Tsoka
17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo. 18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa, 19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati,
“Odala ndinu amene ndi osauka,
chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala
chifukwa mudzakhutitsidwa.
Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala
chifukwa mudzasekerera.
22 Ndinu odala, anthu akamakudani,
kukusalani ndi kukunyozani
ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
24 “Ndinu atsoka, anthu olemera,
popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano,
chifukwa mudzakhala ndi njala.
Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano,
chifukwa mudzabuma ndi kulira.
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani,
popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.