Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 68:1-10

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

68 Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;
    adani ake athawe pamaso pake.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.
    Monga phula limasungunukira pa moto,
    oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
Koma olungama asangalale
    ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;
    iwo akondwere ndi kusangalala.

Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,
    mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;
    dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,
    ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,
    amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;
    koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.

Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,
    pamene munayenda kudutsa chipululu,
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,
    pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.
    Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;
    munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo
    ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

Masalimo 68:19-20

19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu
    amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;
    Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.

Yobu 31:16-23

16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,
    kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha,
    wosagawirako mwana wamasiye,
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,
    ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,
    kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo
    chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,
    poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke,
    mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,
    ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.

Luka 8:40-56

Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu

40 Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera. 41 Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake, 42 chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa.

Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza. 43 Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa. 44 Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.

45 Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?”

Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”

46 Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”

47 Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo. 48 Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”

49 Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”

50 Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”

51 Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo. 52 Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”

53 Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira. 54 Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!” 55 Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya. 56 Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.