Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide. Kupempha.
38 Yehova musandidzudzule mutapsa mtima
kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa,
ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;
mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja
ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha
chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;
tsiku lonse ndimangolira.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,
mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;
ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,
kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;
ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;
anansi anga akhala kutali nane.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,
oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;
tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,
monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Ndakhala ngati munthu amene samva,
amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Ndikudikira Inu Yehova;
mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere
kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Pakuti ndili pafupi kugwa,
ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga;
ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu;
amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino
amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Inu Yehova, musanditaye;
musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza,
Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Phiri la Yehova
4 Mʼmasiku otsiriza,
phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.
Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,
“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,
ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri
ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
kapena kuphunziranso za nkhondo.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa
ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,
ndipo palibe amene adzawachititse mantha,
pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
5 Mitundu yonse ya anthu
itha kutsatira milungu yawo;
ife tidzayenda mʼnjira za Yehova
Mulungu wathu mpaka muyaya.
Cholinga cha Yehova
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti,
“ndidzasonkhanitsa olumala;
ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa
ndiponso amene ndinawalanga.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.
Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.
Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova
kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo,
Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
2 Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
Mulungu Mwini Chitonthozo
3 Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse. 4 Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu. 5 Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri. 6 Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife. 7 Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
8 Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo. 9 Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa. 10 Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe. 11 Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.