Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
68 Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;
adani ake athawe pamaso pake.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.
Monga phula limasungunukira pa moto,
oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 Koma olungama asangalale
ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;
iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,
mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;
dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,
ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,
amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;
koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,
pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,
pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.
Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;
munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo
ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu
amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;
Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
9 Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere;
ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
10 Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala;
amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
11 Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa;
amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
12 Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda,
anthu ovulala akulirira chithandizo.
Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
13 “Pali ena amene amakana kuwala,
amene safuna kuyenda mʼkuwalako
kapena kukhala mʼnjira zake.
14 Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka
ndipo amakapha osauka ndi amphawi;
nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
15 Munthu wachigololo amadikira chisisira;
iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’
ndipo amaphimba nkhope yake.
16 Mbala zimathyola nyumba usiku,
koma masana zimadzitsekera;
izo zimathawa kuwala.
17 Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera.
Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
18 “Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi;
minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo
kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
19 Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana
ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa.
20 Mayi wowabereka amawayiwala,
mphutsi zimasangalala powadya;
anthu oyipa sakumbukiridwanso
koma amathyoka ngati mtengo.
21 Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana,
ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
22 Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake;
ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
23 Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka,
koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
24 Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso;
amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse;
amadulidwa ngati ngala za tirigu.
25 “Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza
ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”
Paulo Adzudzula Petro
11 Petro atafika ku Antiokeya, ine ndinamudzudzula pa gulu chifukwa anapezeka wolakwa. 12 Pakuti asanafike anthu otumidwa ndi Yakobo, iye ankadya pamodzi ndi anthu a mitundu ina. Koma atafika, iyeyo anachoka pakati pa anthuwo nakakhala pa yekha chifukwa ankaopa anthu a mʼgulu la mdulidwe. 13 Ayuda enanso anamutsata pochita zachinyengozi, kotero kuti ngakhale Barnaba anasocheretsedwa chifukwa cha chinyengo chawocho.
14 Koma nditaona kuti iwo sankachita molingana ndi choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinawuza Petro pamaso pa anthu onse kuti, “Iwe ndiwe Myuda koma ukukhala ngati munthu wa mtundu wina, osati Myuda. Nanga nʼchifukwa chiyani ukukakamiza anthu a mitundu ina kuti akhale ngati Ayuda?
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.