Old/New Testament
15 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! 2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,
“ ‘Oyenera kufa adzafa;
oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;
oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;
oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. 4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?
Kodi adzakulira ndani?
Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.
“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.
Choncho Ine ndidzakukanthani.
Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo
monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.
Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga
chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye
kupambana mchenga wa kunyanja.
Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna
dzuwa lili pamutu.
Mwadzidzidzi ndinawagwetsera
kuwawa mtima ndi mantha.
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka
ndipo akupuma wefuwefu.
Dzuwa lake lalowa ukanali usana;
anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.
Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo
kuti awaphe ndi lupanga,”
akutero Yehova.
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,
munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!
Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,
komatu aliyense akunditemberera.
11 Yehova anati,
“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.
Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka
ndi ya mavuto awo.
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,
makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Anthu ako ndi chuma chako
ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,
chifukwa cha machimo anu onse
a mʼdziko lanu lonse.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu
mʼdziko limene inu simulidziwa,
chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto
umene udzakutenthani.”
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;
kumbukireni ndi kundisamalira.
Ndilipsireni anthu ondizunza.
Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.
Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.
Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.
Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,
sindinasangalale nawo anthu amenewo.
Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine
ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?
Bwanji chilonda changa sichikupola?
Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,
kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti,
“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso
ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.
Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,
udzakhalanso mneneri wanga.
Anthu adzabwera kwa iwe
ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba
ngati mkuwa kwa anthu awa.
Adzalimbana nawe
koma sadzakugonjetsa,
pakuti Ine ndili nawe
kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”
akutero Yehova.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
Tsiku la Masautso
16 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, 2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano 3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno, 4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.” 6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo. 7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo. 9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’ 11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa. 12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine. 13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’ ”
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’ 15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe. 17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa. 18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa,
pothawirapo panga nthawi ya masautso,
anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu
kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti,
“Makolo anthu anali ndi milungu yonama,
anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu?
Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa,
kokha kano kuti adziwe
za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga.
Pamenepo adzadziwa kuti
dzina langa ndi Yehova.
17 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo,
lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi.
Uchimowo walembedwa pa mitima yawo
ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 Ngakhale ana awo amakumbukira
maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera,
pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri,
pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense
ndidzazipereka kwa ofunkha
kuti zikhale dipo lawo
chifukwa cha machimo
ochitika mʼdziko lonse.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani
kuti likhale cholowa chanu.
Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu
mʼdziko limene inu simukulidziwa,
chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto,
ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 Yehova akuti,
“Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake,
amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize
pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu;
iye sadzapeza zabwino.
Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi,
mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova,
amene amatsamira pa Iye.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi
umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje.
Mtengowo suopa pamene kukutentha;
masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse.
Suchita mantha pa chaka cha chilala
ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse
ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika.
Ndani angathe kuwumvetsa?
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima
ndi kuyesa maganizo,
ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake
ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo
ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire.
Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera,
ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero
wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli,
onse amene amakusiyani adzachita manyazi.
Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi
chifukwa anakana Yehova,
kasupe wa madzi amoyo.
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira;
pulumutseni ndipo ndidzapulumuka,
chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 Anthu akumandinena kuti,
“Mawu a Yehova ali kuti?
Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange.
Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka.
Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 Musandichititse mantha;
ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 Ondizunza anga achite manyazi,
koma musandichititse manyazi;
iwo achite mantha kwambiri,
koma ine mundichotsere manthawo.
Tsiku la mavuto liwafikire;
ndipo muwawononge kotheratu.
Kusunga Tsiku la Sabata
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu. 20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’ 21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu. 22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu. 23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga. 24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli. 25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya. 26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova. 27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’ ”
2 Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu. 2 Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena. 3 Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu. 4 Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira. 5 Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo. 6 Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola. 7 Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
8 Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino 9 umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo. 10 Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha.
11 Mawu oyenera kuwadalira ndi awa:
Ngati ife tinafa naye pamodzi,
tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
12 Ngati tinapirira,
tidzalamuliranso naye pamodzi.
Ngati ife timukana,
Iye adzatikananso.
13 Ngati ndife osakhulupirika,
Iye adzakhalabe wokhulupirika
popeza sangathe kudzikana.
Kuthana ndi Aphunzitsi Onyenga
14 Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo. 15 Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola. 16 Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera. 17 Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto. 18 Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena. 19 Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
20 Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba. 21 Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
22 Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa. 23 Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano. 24 Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa. 25 Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi. 26 Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.