Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 56-58

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

56 Yehova akuti,

“Chitani chilungamo
    ndi zinthu zabwino,
chifukwa chipulumutso changa chili pafupi
    ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,
    munthu amene amalimbika kuzichita,
amene amasunga Sabata osaliyipitsa,
    ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,
    “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”
Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,
    “Ine ndine mtengo wowuma basi.”

Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,
    nachita zokomera Ine
    ndi kusunga pangano langa,
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino
    mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,
    kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.
Ndidzawapatsa dzina labwino,
    losatha ndi losayiwalika.”
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,
    motero kuti amamutumikira Iye,
amakonda dzina la Yehova,
    amamugwirira ntchito,
komanso kusunga Sabata osaliyipitsa
    ndi kusunga bwino pangano langa,
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,
    ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.
Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo
    ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.
Paja nyumba yanga idzatchedwa
    nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa
    Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,
“Ndidzasonkhanitsano anthu ena
    kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,
    inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,
    onse ndi opanda nzeru;
onse ndi agalu opanda mawu,
    samatha kuwuwa:
amagona pansi nʼkumalota
    amakonda kugona tulo.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;
    sakhuta konse.
Abusa nawonso samvetsa zinthu;
    onse amachita monga akufunira,
    aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!
    Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!
Mawa lidzakhala ngati leroli,
    kapena kuposa lero lino.”
57 Anthu olungama amafa,
    ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;
anthu odzipereka amatengedwa,
    ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.
Anthu olungama amatengedwa
    kuti tsoka lisawagwere.
Iwo amene amakhala moyo wolungama
    amafa mwamtendere;
    amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.

“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,
    inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
Kodi inu mukuseka yani?
    Kodi mukumunena ndani
    ndi kupotoza pakamwa panu?
Kodi inu si ana owukira,
    zidzukulu za anthu abodza?
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,
    ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.
Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa
    ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.
    Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,
ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.
    Kodi zimenezi
    zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.
    Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Mʼnyumba mwanu mwayika
    mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.
Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.
    Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,
ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.
    Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta
    ndi zonunkhira zochuluka.
Munachita kutumiza akazembe anu kutali;
    inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu,
    koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’
Munapezako kumeneko zokhumba zanu
    nʼchifukwa chake simunalefuke.

11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,
    kotero kuti mwakhala mukundinamiza,
ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,
    kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?
Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti
    ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,
    ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo,
    mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!
Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,
    mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.
Koma munthu amene amadalira ine
    adzalandira dziko lokhalamo.
    Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”

Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima

14 Ndipo panamveka mawu akuti,

“Undani, undani, konzani msewu!
    Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,
    amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,
akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,
    koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima
kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse
    ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya
    kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,
popeza kuti ndinalenga anthu anga
    ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;
    ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,
    koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;
    kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19     anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.
Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”
    “Ndipo ndidzawachiritsa.”
            Akutero Yehova.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,
    yosatha kukhala bata,
    mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

Kusala Kwenikweni

58 “Fuwula kwambiri, usaleke.
    Mawu ako amveke ngati lipenga.
Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;
    uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;
    amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,
kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola
    ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.
Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo
    ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala
    kudya pamene Inu simukulabadirapo?
Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa
    pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,
    ndipo mumazunza antchito anu onse.
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,
    mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.
Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,
    kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?
Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango
    ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?
Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,
    tsiku lokondweretsa Yehova?

“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:
Kumasula maunyolo ozunzizira anthu
    ndi kumasula zingwe za goli,
kupereka ufulu kwa oponderezedwa
    ndi kuphwanya goli lililonse?
Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?
    Osowa ndi ongoyendayenda,
kodi mwawapatsa malo ogona?
    Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,
    ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;
chilungamo chanu chidzakutsogolerani
    ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;
    mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,
    ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,
    ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,
pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,
    ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;
    adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa
    ndipo adzalimbitsa matupi anu.
Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,
    ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,
    ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;
inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.
    Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

13 “Muzisunga osaphwanya Sabata;
    musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,
tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.
    Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza
posayenda mʼnjira zanu,
    kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,
    ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.
    Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”
            Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

2 Atesalonika 2

Kubwera kwa Munthu Woyipitsitsa

Pa za kubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikumane naye, abale, tikukupemphani kuti musagwedezeke msanga mʼmaganizo kapena kuopsezedwa ndi uneneri, mbiri kapena kalata yokhala ngati yachokera kwa ife, yonena kuti tsiku lija la Ambuye linafika kale. Musalole kuti wina aliyense akunamizeni mwa njira ina iliyonse. Pakuti tsikulo lisanafike, kudzakhala mpatuko waukulu kwambiri, ndipo kudzaoneka munthu woyipitsitsa uja, munthu woyenera kuwonongedwayo. Iyeyo adzatsutsa ndi kudziyika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza. Iyeyo adzadzikhazika mʼNyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.

Kodi simukukumbukira kuti pamene ndinali nanu pamodzi ndinkakuwuzani zimenezi? Ndipo tsopano mukudziwa chimene chikumuletsa kuonekera, koma adzawululika pa nthawi yake yoyenera. Pakuti mphamvu yobisika yoyipitsitsa ikugwira ntchito ngakhale tsopano; koma amene akutchinga mphamvuyo adzapitiriza kutero mpaka pamene wotchingayo adzachotsedwe. Ndipo kenaka woyipitsitsayo adzaonekera, amene Ambuye Yesu adzamugonjetsa ndi mpweya otuluka mʼkamwa mwake ndi kumuwononga ndi ulemerero wa kubwera kwake. Woyipitsitsayo adzabwera ndi mphamvu za Satana. Adzaonetsa mphamvu zake pochita zizindikiro ndi zodabwitsa zachinyengo. 10 Iye adzagwiritsa ntchito mtundu uliwonse wachinyengo kupusitsa amene akuwonongeka. Iwo akuwonongeka chifukwa akukana kukonda choonadi ndi kuti apulumutsidwe. 11 Chifukwa cha chimenechi, Mulungu akuwatumizira chinyengo chachikulu kuti akhulupirire bodza. 12 Choncho adzalangidwa onse amene sanakhulupirire choonadi, koma anakondwera mu zoyipa.

Imani Mwamphamvu

13 Koma tiyenera kuyamika Mulungu chifukwa cha inu abale okondedwa mwa Ambuye, pakuti Mulungu anakusankhani pachiyambi pomwe kuti mupulumuke chifukwa cha ntchito yoyeretsa ya Mzimu ndi chikhulupiriro chanu mʼchoonadi. 14 Iye anakuyitanirani zimenezi kudzera mwa uthenga wathu wabwino, kuti mulandire nawo ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu. 15 Kotero tsono, abale, imani mwamphamvu ndi kugwiritsa ziphunzitso zimene tinakupatsani kudzera mʼmawu apakamwa kapena kudzera mʼkalata.

16 Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, 17 akulimbikitseni ndi kukupatsani mphamvu yogwirira ntchito ndi kuyankhula zabwino zilizonse.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.