Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 53-55

53 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi;
    kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake,
    ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma.
Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira,
    analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,
    munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,
ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.
    Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.

Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;
    ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.
Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,
    kumukantha ndi kumusautsa.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,
    ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;
iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,
    ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,
    aliyense mwa ife akungodziyendera;
ndipo Yehova wamusenzetsa
    zoyipa zathu zonse.

Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,
    koma sanayankhule kanthu.
Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,
    kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,
    momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha.
    Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake,
poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?
    Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa
    ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma,
ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa,
    kapena kuyankhula za chinyengo.

10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa.
    Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa.
Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali,
    ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Atatha mazunzo a moyo wake,
    adzaona kuwala, ndipo adzakhutira.
Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri,
    popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu,
    adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,
popeza anapereka moyo wake mpaka kufa,
    ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe.
Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri,
    ndipo anawapempherera anthu olakwa.

Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni

54 “Sangalala, iwe mayi wosabala,
    iwe amene sunabalepo mwana;
imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,
    iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
    kuposa mkazi wokwatiwa,”
            akutero Yehova.
Kulitsa malo omangapo tenti yako,
    tambasula kwambiri nsalu zake,
    usaleke;
talikitsa zingwe zako,
    limbitsa zikhomo zako.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;
    ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina
    ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.

“Usachite mantha; sadzakunyozanso.
    Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.
Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako
    ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;
    dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Yehova wakuyitananso,
    uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,
mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”
    akutero Mulungu wako.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,
    koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa
    ndili wokwiya kwambiri.
Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,
    ndidzakuchitira chifundo,”
    akutero Yehova Mpulumutsi wako.

“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.
    Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.
Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,
    sindidzakudzudzulaninso.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka
    ndi zitunda kusunthidwa,
koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.
    Pangano langa lamtendere silidzasintha,”
    akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.

11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza,
    Ine ndidzakongoletsa miyala yako.
    Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi.
    Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto,
    ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse,
    ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni:
Sudzakhalanso wopanikizika,
    chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse.
Sudzakhalanso ndi mantha
    chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa;
    aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.

16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo
    amene amakoleza moto wamakala
    ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito.
Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17     palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,
    ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.
Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.
    Chipambano chawo chichokera kwa Ine,”
            akutero Yehova.

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

55 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,
    bwerani madzi alipo;
ndipo inu amene mulibe ndalama
    bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!
Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka
    osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,
    ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?
Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;
    ndipo mudzisangalatse.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;
    mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.
Ndidzachita nanu pangano losatha,
    chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,
    kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,
    ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.
Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,
    Woyerayo wa Israeli,
    wakuvekani ulemerero.”

Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.
    Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,
    ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.
Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,
    ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,
    ngakhale njira zanu si njira zanga,”
            akutero Yehova.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,
    momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,
    ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana
    zimatsika kuchokera kumwamba,
ndipo sizibwerera komweko
    koma zimathirira dziko lapansi.
Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera
    kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.
    Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,
koma adzachita zonse zimene ndifuna,
    ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe
    ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;
mapiri ndi zitunda
    zidzakuyimbirani nyimbo,
ndipo mitengo yonse yamʼthengo
    idzakuwombereni mʼmanja.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,
    ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.
Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,
    ngati chizindikiro chamuyaya,
    chimene sichidzafafanizika konse.”

2 Atesalonika 1

Paulo, Silivano ndi Timoteyo.

Kulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Chisomo ndi mtendere kwa inu kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.

Kuyamika ndi Pemphero

Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe. Nʼchifukwa chake, timayankhula monyadira mʼmipingo yonse ya Mulungu za kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pakati pa masautso onse ndi mayesero amene mukudutsamo.

Zonsezi zikutsimikiza kuti Mulungu amaweruza molungama. Zotsatira zake ndi zakuti mudzatengedwa kukhala oyenera kulowa mu ufumu wa Mulungu umene mukuwuvutikira. Mulungu ndi wolungama ndipo adzalanga amene amakusautsaniwo ndikukupatsani mpumulo amene mukusautsidwa, pamodzi ndi ifenso. Izi zidzachitika Ambuye Yesu akadzaoneka mʼmalawi amoto kuchokera kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu. Iye adzalanga amene sadziwa Mulungu ndi amene samvera Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu. Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake 10 pa tsiku limene iye adzabwera kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ndi kuyamikidwa ndi onse amene anakhulupirira. Inu mudzakhala nawo mʼgulumo chifukwa munakhulupirira umboni wathu.

11 Nʼchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera mayitanidwe ake, ndi kuti mwa mphamvu zake akwaniritse cholinga chanu chilichonse chabwino ndi chilichonse chochitika mwachikhulupiriro. 12 Ife timapempherera zimenezi kuti dzina la Ambuye athu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mulemekezedwe mwa Iyeyo. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha chisomo cha Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.