Old/New Testament
Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki
50 Yehova akuti,
“Kalata imene ndinasudzulira amayi
anu ili kuti?
Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,
ndinakugulitsani kwa ati?
Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;
amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?
Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?
Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?
Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?
Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,
mitsinje ndinayisandutsa chipululu;
nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;
ndipo zinafa ndi ludzu.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima
ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula
kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.
Mmawa mulimonse amandidzutsa,
amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,
ndipo sindinakhale munthu wowukira
ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya
masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;
sindinawabisire nkhope yanga
anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,
sindidzachita manyazi.
Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,
chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,
ndaninso amene adzandiyimba mlandu?
Abwere kuti tionane maso ndi maso!
Mdani wanga ndi ndani?
Abweretu kuti tilimbane!
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.
Ndaninso amene adzanditsutsa?
Onse adzatha ngati chovala
chodyedwa ndi njenjete.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova
ndi kumvera mawu a mtumiki wake?
Aliyense woyenda mu mdima,
popanda chomuwunikira,
iye akhulupirire dzina la Yehova
ndi kudalira Mulungu wake.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto
ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,
lowani mʼmoto wanu womwewo.
Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.
Ndipo ine Yehova
ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni
51 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso
ndiponso amene mumafunafuna Yehova:
Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa
ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu,
ndi Sara, amene anakubalani.
Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,
koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni,
ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;
Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,
malo ake owuma ngati munda wa Yehova.
Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda
ndi kundiyamika.
4 “Mverani Ine, anthu anga:
tcherani khutu, inu mtundu wanga:
malangizo adzachokera kwa Ine;
cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.
Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;
ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.
Mayiko akutali akundiyembekezera.
Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Kwezani maso anu mlengalenga,
yangʼanani pansi pa dziko;
mlengalenga udzazimirira ngati utsi,
dziko lapansi lidzatha ngati chovala
ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.
Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,
chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,
anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;
musaope kudzudzulidwa ndi anthu
kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;
mbozi idzawadya ngati thonje.
Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,
chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,
Inu Yehova;
dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,
monga nthawi ya mibado yakale.
Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,
amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,
madzi ozama kwambiri aja?
Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,
kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera
nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;
chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.
Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,
chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.
Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?
Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,
amene anayala za mlengalenga
ndi kuyika maziko a dziko lapansi.
Inu nthawi zonse mumaopsezedwa
chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani
amene angofuna kukuwonongani.
Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;
sadzalowa mʼmanda awo,
kapena kusowa chakudya.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.
Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu
ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.
Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,
ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,
ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”
Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu
17 Dzambatuka, dzambatuka!
Imirira iwe Yerusalemu.
Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo
chimene Yehova anakupatsa.
Iwe amene unagugudiza
chikho chochititsa chizwezwe.
18 Mwa ana onse amene anabereka,
panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;
mwa ana onse amene analera,
panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe.
Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.
Ndani angakumvere chisoni?
Ndani angakutonthoze?
20 Ana ako akomoka;
ali lambalamba pa msewu,
ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.
Ukali wa Yehova
ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,
iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Ambuye Yehova wanu,
Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,
“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako
chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;
sudzamwanso chikho
cha ukali wanga.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,
amene ankakuwuza kuti,
‘gona pansi tikuyende pa msana.’
Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,
ngati msewu woti ayendepo.”
52 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni,
vala zilimbe.
Vala zovala zako zokongola,
iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika.
Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa
sadzalowanso pa zipata zako.
2 Sasa fumbi lako;
imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu.
Inu omangidwa a ku Ziyoni,
masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
3 Pakuti Yehova akuti,
“Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani,
choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti,
“Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto;
nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti,
“Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu,
amene amawalamulira amawanyoza,”
akutero Yehova.
“Ndipo tsiku lonse, akungokhalira
kuchita chipongwe dzina langa.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa;
kotero adzadziwa
kuti ndi Ine amene ndikuyankhula,
Indedi, ndine.”
7 Ngokongoladi mapazi a
amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.
Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,
chisangalalo ndi chipulumutso.
Iwo akubwera kudzawuza anthu
a ku Ziyoni kuti,
“Mulungu wako ndi mfumu!”
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;
akuyimba pamodzi mwachimwemwe.
Popeza akuona chamaso
kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,
inu mabwinja a Yerusalemu,
pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
wapulumutsa Yerusalemu.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika
pamaso pa anthu a mitundu yonse,
ndipo anthu onse a dziko lapansi
adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko!
Musakhudze kanthu kodetsedwa!
Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova
tulukanimo ndipo mudziyeretse.
12 Koma simudzachoka mofulumira
kapena kuchita chothawa;
pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu,
Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Kuzunzika ndi Ulemerero wa Mtumiki
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake
adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,
chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.
Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,
ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.
Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,
ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
Tsiku la Ambuye
5 Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2 chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3 Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5 Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6 Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7 Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8 Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9 Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10 Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11 Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
Malangizo Otsiriza
12 Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13 Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14 Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15 Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
16 Kondwerani nthawi zonse. 17 Pempherani kosalekeza. 18 Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
19 Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20 Musanyoze mawu a uneneri. 21 Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22 Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24 Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 Abale, mutipempherere. 26 Perekani moni wachikondi kwa onse. 27 Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.