Old/New Testament
Mulungu Thandizo la Israeli
41 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!
Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;
tiyeni tikhale pamodzi
kuti atiweruze.
2 “Ndani anadzutsa wochokera kummawa
uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?
Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake
ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa
ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi
nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Amawalondola namayenda mosavutika,
mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,
si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?
Ine Yehova, ndine chiyambi
ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;
anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.
Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 aliyense akuthandiza mnzake
ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,
ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo
amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.
Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”
Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 “Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,
Yakobo amene ndakusankha,
Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,
ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.
Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’
Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;
usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.
Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,
ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 “Onse amene akupsera mtima
adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;
onse amene akukangana nawe
sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Udzafunafuna adani ako,
koma sadzapezeka.
Iwo amene akuchita nawe nkhondo
sadzakhalanso kanthu.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,
amene ndikukugwira dzanja lako lamanja
ndipo ndikuti, usaope;
ndidzakuthandiza.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,
iwe wochepa mphamvu Israeli,
chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”
akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu
chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.
Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,
ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso
adzamwazika ndi kamvuluvulu.
Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,
ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,
koma sakuwapeza;
ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.
Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;
Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,
ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.
Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi
ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Mʼchipululu ndidzameretsa
mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi.
Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo
ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 kuti anthu aone ndi kudziwa;
inde, alingalire ndi kumvetsa,
kuti Yehova ndiye wachita zimenezi;
kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 “Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’
Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze
zomwe zidzachitike mʼtsogolo.
Tifotokozereni zinthu zamakedzana
tiziganizire
ndi kudziwa zotsatira zake.
Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,
ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu.
Chitani chinthu chabwino kapena choyipa,
ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Koma inu sindinu kanthu
ndipo zochita zanu nʼzopandapake;
amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 “Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,
munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana.
Amapondaponda olamulira ngati matope,
ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,
kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’
Palibe amene ananena,
palibe analengeza zimenezi,
palibe anamva mawu anu.
27 Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’
Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,
palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu,
palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!
Zochita zawo si kanthu konse;
mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.
Mtumiki wa Yehova
42 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,
amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.
Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,
ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,
kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola,
ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.
Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa
mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,
ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
5 Yehova Mulungu
amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,
amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,
amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,
ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;
ndikugwira dzanja ndipo
ndidzakuteteza.
Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu
ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
7 Udzatsekula maso a anthu osaona,
udzamasula anthu a mʼndende
ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!
Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense
kapena matamando anga kwa mafano.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,
ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;
zinthuzo zisanaonekere
Ine ndakudziwitsani.”
Nyimbo Yotamanda Yehova
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,
inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.
Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;
midzi ya Akedara ikondwere.
Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;
afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Atamande Yehova
ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,
adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;
akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo
ndipo adzagonjetsa adani ake.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,
ndakhala ndili phee osachita kanthu.
Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,
ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda
ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;
ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba
ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,
ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;
ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala
ndipo ndidzasalaza malo osalala.
Zimenezi ndizo ndidzachite;
sindidzawataya.
17 Koma onse amene amadalira mafano
amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’
ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
Aisraeli Alephera Kuphunzira
18 “Imvani, agonthi inu;
yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?
Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?
Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,
kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;
makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 Chinamukomera Yehova
chifukwa cha chilungamo chake,
kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,
onsewa anawakola mʼmaenje
kapena akuwabisa mʼndende.
Tsono asanduka chofunkha
popanda wina wowapulumutsa
kapena kunena kuti,
“Abwezeni kwawo.”
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi
kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,
ndi Israeli kwa anthu akuba?
Kodi si Yehova,
amene ife tamuchimwirayu?
Pakuti sanathe kutsatira njira zake;
ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Motero anawakwiyira kwambiri,
nawavutitsa ndi nkhondo.
Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;
motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
1 Paulo, Silivano ndi Timoteyo.
Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.
Chisomo ndi mtendere kwa inu.
Kuyamikira Chikhulupiriro cha Atesalonika
2 Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu. 3 Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani, 5 chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni. 6 Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera. 7 Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya. 8 Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu, 9 pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona. 10 Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.