Old/New Testament
Chiweruzo cha Anthu a Mitundu Yonse
34 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve:
tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse:
Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,
dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse;
wapsera mtima magulu awo onse ankhondo.
Iye adzawawononga kotheratu,
nawapereka kuti aphedwe.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja,
mitembo yawo idzawola ndi kununkha;
mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka
ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala;
nyenyezi zonse zidzayoyoka
ngati masamba ofota a mphesa,
ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba;
taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu,
anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi,
lakutidwa ndi mafuta;
magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi,
mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna.
Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira
ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati,
ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe.
Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha,
ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira
ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula,
ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule;
dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana;
utsi wake udzafuka kosalekeza.
Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado;
palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu;
amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo.
Mulungu adzatambalitsa pa Edomu
chingwe choyezera cha chisokonezo
ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko;
akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa,
khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake.
Ankhandwe azidzadya mʼmenemo;
malo okhalamo akadzidzi.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi,
ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana.
Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa
ndi kupeza malo opumulirako.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira,
adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake;
akamtema adzasonkhananso kumeneko,
awiriawiri.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga:
mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa;
sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake.
Pakuti Yehova walamula kuti zitero,
ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Yehova wagawa dziko lawo;
wapatsa chilichonse chigawo chake.
Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya
ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
Chimwemwe cha Opulumutsidwa
35 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;
dziko lowuma lidzakondwa
ndi kuchita maluwa. 2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka
lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.
Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,
maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.
Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,
ukulu wa Mulungu wathu.
3 Limbitsani manja ofowoka,
limbitsani mawondo agwedegwede;
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti;
“Limbani mtima, musachite mantha;
Mulungu wanu akubwera,
akubwera kudzalipsira;
ndi kudzabwezera chilango adani anu;
akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso
ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,
ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.
Akasupe adzatumphuka mʼchipululu
ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe,
nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.
Pamene panali mbuto ya ankhandwe
padzamera udzu ndi bango.
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;
ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.
Anthu odetsedwa
sadzayendamo mʼmenemo;
zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Kumeneko sikudzakhala mkango,
ngakhale nyama yolusa sidzafikako;
sidzapezeka konse kumeneko.
Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.
Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;
kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.
Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,
ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.
Senakeribu Awopseza Yerusalemu
36 Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda. 2 Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala. 3 Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,
“Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani? 5 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? 6 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira. 7 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 “Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! 9 Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo. 10 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 14 Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni! 15 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 17 mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 “Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 19 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 20 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.
2 Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso. 2 Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu. 3 Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso. 4 Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake. 5 Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
Za Moyo Weniweni mwa Khristu
6 Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo. 7 Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
8 Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
9 Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu. 10 Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse. 11 Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija. 12 Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
13 Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse. 14 Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda. 15 Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
Ufulu Wathu
16 Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata. 17 Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu. 18 Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu. 19 Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
20 Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa: 21 “Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?” 22 Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe. 23 Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.