Old/New Testament
Tsoka kwa Efereimu
28 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu.
Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa
limene lili pa mutu pa anthu
oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga.
Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga,
ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho;
ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera
a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa
lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja,
udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa
imene munthu akangoyiona amayithyola
nthawi yokolola isanakwane.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse
adzakhala ngati nkhata yaufumu,
chipewa chokongola
kwa anthu ake otsala.
6 Iye adzapereka mtima
wachilungamo kwa oweruza,
adzakhala chilimbikitso kwa
amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo
ndipo akusochera chifukwa cha mowa:
ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa
ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo;
akusochera chifukwa cha mowa,
akudzandira pamene akuona masomphenya,
kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha
ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani?
Uthengawu akufuna kufotokozera yani?
Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa,
kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono
lemba ndi lemba, mzere ndi mzere,
phunziro ndi phunziro.
Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino.
Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 anakuwuzani kuti,
“Malo opumulira ndi ano,
otopa apumule, malo owusira ndi ano.”
Koma inu simunamvere.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani
pangʼonopangʼono lemba ndi lemba,
mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro.
Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo,
adzapweteka ndi kukodwa mu msampha
ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova,
inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa,
ife tachita mgwirizano ndi manda.
Pamene mliri woopsa ukadzafika
sudzatikhudza ife,
chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu
ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.”
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi:
“Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri
ngati maziko mu Ziyoni,
mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu;
munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake,
ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere;
matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza,
ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa;
mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa.
Pakuti mliri woopsa udzafika,
ndipo udzakugonjetsani.
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani.
Udzafika mmawa uliwonse,
usiku ndi usana.”
Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu
adzaopsedwa kwambiri.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo;
ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu
adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni;
adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo,
ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Tsopano lekani kunyoza,
mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri;
Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti,
“Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga;
mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha?
Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Pamene iye wasalaza mundawo,
kodi samafesa mawere ndi chitowe?
Kodi suja samadzala tirigu
ndi barele mʼmizere yake,
nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Mulungu wake amamulangiza
ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero,
kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta;
mawere amapuntha ndi ndodo
ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi,
komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke.
Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta,
koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,
wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
Tsoka kwa Mzinda wa Davide
29 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,
mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!
Papite chaka chimodzi kapena ziwiri
ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli
ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,
mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;
ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo
ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,
mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,
adzamveka ngati a mzukwa.
Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.
Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.
Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera
ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,
kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli
nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,
chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,
gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,
koma podzuka ali nayobe njala;
kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,
koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.
Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse
chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.
Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,
ledzerani, koma osati ndi vinyo,
dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.
Watseka maso anu, inu aneneri;
waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 Ambuye akuti,
“Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo,
ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo,
koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso.
Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira
kuwachitira ntchito zodabwitsa;
nzeru za anthu anzeru zidzatha,
luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Tsoka kwa amene amayesetsa
kubisira Yehova maganizo awo,
amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti,
“Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Inu mumazondotsa zinthu
ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya.
Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti
“Sunandipange ndi iwe?”
Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti,
“Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde,
ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku,
ndipo anthu osaona amene
ankakhala mu mdima adzapenya.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova;
ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira,
oseka anzawo sadzaonekanso,
ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa,
kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu
ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti,
“Anthu anga sadzachitanso manyazi;
nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 Akadzaona ana awo ndi
ntchito ya manja anga pakati pawo,
adzatamanda dzina langa loyera;
adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo,
ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru;
onyinyirika adzalandira malangizo.”
Osakhulupirira za Thupi
3 Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.
2 Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. 3 Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi 4 ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.
Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. 5 Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. 6 Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.
7 Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. 8 Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu 9 ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10 Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11 kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.
Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro
12 Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.
Kutsanzira Paulo
15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.
17 Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18 Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19 Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20 Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21 Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.