Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 17-19

Uthenga Wotsutsa Damasiko

17 Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,
    koma udzasanduka bwinja.
Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu
    ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi
    popanda wina woziopseza.
Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,
    ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;
Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu
    monga anthu a ku Israeli,”
            akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;
    ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu
    umene anatsiriza kukolola.
Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu
    anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale
    monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni
kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi
    mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”
            akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo
    ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,
    ntchito ya manja awo,
ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,
    ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10 Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;
    simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.
Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,
    ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11 nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo
    ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,
komabe zimenezi sizidzakupindulirani
    pa tsiku la mavuto.

12 Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,
    akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!
Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,
    akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13 Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,
    koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.
Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,
    ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14 Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,
    ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.
Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,
    gawo la amene amatibera zinthu zathu.

Za Kulangidwa kwa Kusi

18 Tsoka kwa anthu a ku Kusi.
    Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo,
    mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi,
ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro,
kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala,
    ndi woopedwa ndi anthu.
Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena.
    Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”

Inu nonse anthu a pa dziko lonse,
    inu amene mumakhala pa dziko lapansi,
pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri
    yangʼanani,
ndipo pamene lipenga lilira
    mumvere.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti,
    “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana,
monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha,
    monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka
    ndiponso mphesa zitayamba kupsa,
Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira,
    ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama
    ndiponso zirombo zakuthengo;
mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe,
    ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.

Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse,

zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala,
    kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe,
mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo,
    anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.

Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Igupto

19 Uthenga onena za Igupto:

Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro,
    ndipo akupita ku Igupto.
Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake,
    ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.

“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha;
    mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake,
    mnansi ndi mnansi wake,
    mzinda ndi mzinda unzake,
    ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
Aigupto adzataya mtima
    popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo;
adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
    kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
Ndidzawapereka Aigupto
    kwa olamulira ankhanza,
ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,”
    akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa,
    ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
Ngalande zake zidzanunkha;
    ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma.
Bango ndi dulu zidzafota,
    ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo
    ndi ku mathiriro a mtsinjewo.
Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo
    zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula,
    onse amene amaponya mbedza mu Nailo;
onse amene amaponya makoka mʼmadzi
    adzalira.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima,
    anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi,
    ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.

11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru;
    aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa.
Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti,
    “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru,
    wophunzira wa mafumu akale?”

12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti?
    Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa
zimene Yehova Wamphamvuzonse
    wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru,
    atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa;
atsogoleri a dziko la Igupto
    asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Yehova wasocheretsa
    anthu a ku Igupto.
Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita,
    ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite,
    mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.

16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga. 17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.

18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.

19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso. 20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa. 21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo. 22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.

23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi. 24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi. 25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

Aefeso 5:17-33

17 Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite. 18 Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera. 19 Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu. 20 Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

Malangizo kwa Akazi ndi Amuna Mʼbanja

21 Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.

22 Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye. 23 Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake. 24 Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.

25 Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo 26 kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake. 27 Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro. 28 Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha. 29 Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake 30 pakuti ndife ziwalo za thupi lake. 31 “Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.” 32 Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo. 33 Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.