Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 9-10

Ufumu wa Mesiya

Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.

Anthu oyenda mu mdima
    awona kuwala kwakukulu;
kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani
    kuwunika kwawafikira.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu
    ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo.
Iwo akukondwa pamaso panu,
    ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola,
ngatinso mmene anthu amakondwera
    pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani,
    inu mwathyola goli
limene limawalemera,
    ndodo zimene amamenyera mapewa awo,
    ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo,
    ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi
zidzatenthedwa pa moto
    ngati nkhuni.
Chifukwa mwana watibadwira,
    mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife,
    ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake.
Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti
    Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,
    Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
Ulamuliro ndi mtendere wake
    zidzakhala zopanda malire.
Iye adzalamulira ufumu wake ali pa
    mpando waufumu wa Davide,
ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza
    mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo
    kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya.
Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse
    watsimikiza kuchita zimenezi.

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo;
    ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Anthu onse okhala mu
    Efereimu ndi okhala mu Samariya,
adzadziwa zimenezi.
    Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Ngakhale njerwa zagumuka,
    koma ife tidzamanga ndi miyala yosema.
Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa,
    koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo
    ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo
    ayasama pakamwa kuti adye a Israeli.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja,
    ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe,
    nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka,
    mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa,
    ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata,
    ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye,
pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo
    aliyense amayankhula zopusa.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto;
    moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga,
umayatsa nkhalango yowirira,
    ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse,
    dziko lidzatenthedwa
ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto;
    palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya,
    koma adzakhalabe ndi njala;
kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya,
    koma sadzakhuta.
Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21     Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase;
    onsewa pamodzi adzadya Yuda.

Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

10 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
    kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
    ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,
amalanda zinthu za akazi amasiye
    ndi kubera ana amasiye.
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
    pofika chiwonongeko chochokera kutali?
Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?
    Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
    kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.
Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

Chiweruzo cha Mulungu pa Asiriya

“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,
    iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,
    ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine,
kukafunkha ndi kulanda chuma,
    ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
Koma izi si zimene akufuna kukachita,
    izi si zimene zili mʼmaganizo mwake;
cholinga chake ndi kukawononga,
    kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
    ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?
Kodi Hamati sali ngati Aripadi,
    nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,
    mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake
    monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’ ”

12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake. 13 Pakuti mfumuyo ikuti,

“ ‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa,
    ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu.
Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu,
    ndinafunkha chuma chawo;
    ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu
    ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame,
ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa,
    motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse;
palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake,
    kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’ ”

15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,
    kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito?
Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula,
    kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
    adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu;
kunyada kwa mfumuyo kudzapsa
    ndi moto wosazima.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,
    Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto.
Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza
    ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa
    ngati nkhalango yayikulu
    ndi ngati nthaka yachonde.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,
    yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.

Aisraeli Otsala

20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,
    opulumuka a nyumba ya Yakobo,
sadzadaliranso anthu
    amene anawakantha,
koma adzadalira Yehova,
    Woyerayo wa Israeli.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo
    adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,
    otsala okha ndiwo adzabwerere.
Chiwonongeko chalamulidwa,
    chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse
    monga momwe analamulira.

24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,

“Inu anthu anga okhala mu Ziyoni,
    musawaope Asiriya,
amene amakukanthani ndi ndodo
    nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu
    ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”

26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,
    monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu;
ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi
    ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,
    goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu;
golilo lidzathyoka
    chifukwa cha kunenepa kwambiri.

28 Adani alowa mu Ayati
    apyola ku Migironi;
    asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,
    “Tikagona ku Geba”
Rama akunjenjemera;
    Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!
    Tchera khutu, iwe Laisa!
    Iwe Anatoti wosauka!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa;
    anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;
    adzagwedeza mikono yawo,
kuopseza anthu a ku Ziyoni,
    pa phiri la Yerusalemu.

33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
    adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo,
mitengo yodzikweza idzadulidwa,
    mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;
    Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

Aefeso 3

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.