Old/New Testament
Chiweruzo pa Yerusalemu ndi Yuda
3 Taonani tsopano, Ambuye
Yehova Wamphamvuzonse,
ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda
zinthu pamodzi ndi thandizo;
adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,
oweruza ndi aneneri,
anthu olosera ndi akuluakulu,
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,
aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;
ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 Anthu adzazunzana,
munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.
Anthu wamba adzanyoza
akuluakulu.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake
mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,
“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;
lamulira malo opasuka ano!”
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,
“Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.
Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;
musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 Yerusalemu akudzandira,
Yuda akugwa;
zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,
sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;
amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;
salibisa tchimo lawolo.
Tsoka kwa iwo
odziputira okha mavuto.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,
pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!
Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga,
ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.
Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;
akukuchotsani pa njira yanu.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;
wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 Yehova akuwazenga milandu
akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:
“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;
nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,
nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”
Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 Yehova akunena kuti,
“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,
akuyenda atakweza makosi awo,
akukopa amuna ndi maso awo
akuyenda monyangʼama
akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;
Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi, 19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope, 20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa, 21 mphete ndi zipini, 22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama, 23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha,
mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe;
mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi;
mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli;
mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga,
asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira;
Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
4 Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri
adzagwira mwamuna mmodzi,
nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu,
ndi kuvala zovala zathu;
inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu.
Tichotseni manyazi aumbeta!”
Nthambi ya Yehova
2 Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. 3 Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. 4 Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. 5 Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. 6 Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.
Kuchita Zabwino kwa Onse
6 Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2 Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3 Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4 Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5 pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
6 Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
7 Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8 Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9 Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10 Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano
11 Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
12 Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13 Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14 Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15 Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16 Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
17 Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.