Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 1-2

Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!
    Pakuti Yehova wanena kuti,
“Ndinabala ana ndi kuwalera,
    koma anawo andiwukira Ine.
Ngʼombe imadziwa mwini wake,
    bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,
koma Israeli sadziwa,
    anthu anga samvetsa konse.”

Haa, mtundu wochimwa,
    anthu olemedwa ndi machimo,
obadwa kwa anthu ochita zoyipa,
    ana odzipereka ku zoyipa!
Iwo asiya Yehova;
    anyoza Woyerayo wa Israeli
    ndipo afulatira Iyeyo.

Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?
    Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?
Mutu wanu wonse uli ndi mabala,
    mtima wanu wonse wafowokeratu.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu
    palibe pabwino,
paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,
    mabala ali magazi chuchuchu,
mabala ake ngosatsuka, ngosamanga
    ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

Dziko lanu lasanduka bwinja,
    mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;
minda yanu ikukololedwa ndi alendo
    inu muli pomwepo,
    dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha
    ngati nsanja mʼmunda wampesa,
ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,
    ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda
    kutisiyira opulumuka,
tikanawonongeka ngati Sodomu,
    tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10 Imvani mawu a Yehova,
    inu olamulira Sodomu;
mverani lamulo la Mulungu wathu,
    inu anthu a ku Gomora!
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani
    nsembe zanu zochuluka?”
“Zandikola nsembe zanu zopsereza
    za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;
sindikusangalatsidwanso
    ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Ndani anakulamulirani kuti
    mubwere nazo pamaso panga?
    Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!
    Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.
Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,
    kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika
    ndimadana nazo.
Zasanduka katundu wondilemera;
    ndatopa kuzinyamula.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera,
    Ine sindidzakuyangʼanani;
ngakhale muchulukitse mapemphero anu,
    sindidzakumverani.
Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16     sambani, dziyeretseni.
Chotsani pamaso panu
    ntchito zanu zoyipa!
Lekani kuchita zoyipa,
17     phunzirani kuchita zabwino!
Funafunani chilungamo,
    thandizani oponderezedwa.
Tetezani ana amasiye,
    muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18 Yehova akuti,
    “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.
Ngakhale machimo anu ali ofiira,
    adzayera ngati thonje.
Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,
    adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera
    mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 koma mukakana ndi kuwukira
    mudzaphedwa ndi lupanga.”
            Pakuti Yehova wayankhula.

21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika
    wasandukira wadama!
Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;
    mu mzindamo munali chilungamo,
    koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe,
    vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Atsogoleri ako ndi owukira,
    anthu ogwirizana ndi mbala;
onse amakonda ziphuphu
    ndipo amathamangira mphatso.
Iwo sateteza ana amasiye;
    ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,
    Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,
“Haa, odana nane ndidzawatha,
    ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;
    ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,
    monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,
    aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.
Kenaka iweyo udzatchedwa
    mzinda wolungama,
    mzinda wokhulupirika.”

27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,
    anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,
    ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu
    imene inkakusangalatsani;
mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda
    imene munayipatula.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,
    mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,
    ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;
motero zonse zidzayakira limodzi,
    popanda woti azimitse motowo.”

Phiri la Yehova

Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
    kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,
lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
    ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,
    ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
    ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
    mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko,
    ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
    ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
    kapena kuphunziranso za nkhondo.

Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,
    tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

Inu Yehova mwawakana anthu anu,
    nyumba ya Yakobo.
Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;
    amawombeza mawula ngati Afilisti,
    ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;
    ndipo chuma chawo ndi chosatha.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;
    ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;
    iwo amapembedza ntchito ya manja awo,
    amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa
    ndi kutsitsidwa.
    Inu Yehova musawakhululukire.

10 Lowani mʼmatanthwe,
    bisalani mʼmaenje,
kuthawa kuopsa kwa Yehova
    ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha,
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku
    limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,
    ndipo adzagonjetsa
    onse amphamvu,
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,
    ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 tsiku la mapiri onse ataliatali
    ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali
    ndiponso malinga onse olimba,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi
    ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18     ndipo mafano onse adzatheratu.

19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndi mʼmaenje a nthaka,
kuthawa mkwiyo wa Yehova,
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira
    mfuko ndi mileme
mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,
    amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka
kuthawa mkwiyo wa Yehova
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22 Lekani kudalira munthu,
    amene moyo wake sukhalira kutha.
Iye angathandize bwanji wina aliyense?

Agalatiya 5

Ufulu mwa Khristu

Khristu anatimasula kuti tikhale mfulu. Tsono chirimikani, ndipo musakodwenso mʼgoli la ukapolo.

Chonde mvetsetsani! Ine Paulo, ndikukuwuzani kuti mukalola kuchita mdulidwe, Khristu simupindula nayenso konse. Ndikubwerezanso kuwuza munthu aliyense wovomereza kuchita mdulidwe kuti ayeneranso kutsata Malamulo onse. Inu amene mukufuna kulungamitsidwa ndi lamulo mwachotsedwa mwa Khristu; munagwa kusiyana nacho chisomo. Koma mwachikhulupiriro, ife tikudikira mwachidwi kudzera mwa Mzimu, chilungamo chimene tikuyembekeza. Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe kapena kusachita mdulidwe zilibe phindu. Chinthu chokhacho chimene chimafunika ndi chikhulupiriro chogwira ntchito mwachikondi.

Inu munkathamanga mpikisano wanu wabwino. Anakuletsani ndani kuti musamverenso choonadi? Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Iye amene anakuyitanani. “Yisiti wapangʼono amagwira ntchito mu buledi yense.” 10 Ine ndikutsimikiza mwa Ambuye kuti inu simudzasiyana nane maganizo. Iye amene akukusokonezani adzalangidwa, kaya iyeyo ndiye ndani. 11 Abale, ngati ine ndikulalikirabe za mdulidwe, nʼchifukwa chiyani ndikusautsidwabe? Ngati ndikanakhala kuti sindikulalikira chipulumutso cha mtanda, palibe amene akanakhumudwa. 12 Kunena za amene akukuvutani, ndikanakonda akanangodzithena okha!

Moyo mwa Mzimu Woyera

13 Inu abale, Mulungu anakuyitanani kuti mukhale mfulu. Koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo kuchita zoyipa zachikhalidwe cha uchimo cha thupi lanu, koma mutumikirane wina ndi mnzake mwachikondi. 14 Pakuti malamulo onse akuphatikizidwa mu lamulo ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 15 Ngati mupitiriza kulumana ndi kukhadzulana, samalani kuti mungawonongane.

16 Choncho ine ndikuti, mulole kuti Mzimu akutsogolereni ndipo simudzachita zofuna za thupi lanu la uchimo. 17 Pakuti thupi lanu la uchimo limalakalaka zimene ndi zotsutsana ndi Mzimu, ndi Mzimu zimene ndi zotsutsana ndi thupi lanu la uchimo. Ziwirizi zimadana, kotero kuti simungachite zimene mukufuna. 18 Koma ngati Mzimu akutsogolerani, ndiye kuti simuli pansi pa lamulo.

19 Ntchito za thupi lanu la uchimo zimaonekera poyera ndi izi: dama, zodetsa ndi kuchita zonyansa; 20 kupembedza mafano ndi ufiti; kudana, kukangana, kupsa mtima, kudzikonda, kugawikana, mipatuko 21 ndi nsanje, kuledzera, mchezo ndi zina zotere. Ine ndikukuchenjezani monga ndinachita poyamba paja kuti amene amachita zimenezi sadzalandira ufumu wa Mulungu.

22 Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, kukhulupirika, 23 kufatsa ndi kudziretsa. Palibe lamulo loletsa zimenezi. 24 Amene ali ake a Khristu Yesu anapachika pa mtanda thupi lawo la uchimo pamodzi ndi zokhumba zawo ndi zolakalaka zawo. 25 Popeza timakhala ndi moyo mwa Mzimu Woyera, tiyeni tiyende pamodzi ndi Mzimu Woyera. 26 Tisakhale odzitukumula, oputana ndi ochitirana nsanje.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.