Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Nyimbo ya Solomoni 6-8

Abwenzi

Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
    kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?
Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti
    kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,
    ku timinda ta zokometsera zakudya,
akukadyetsa ziweto zake ku minda,
    ndiponso akuthyola maluwa okongola.
Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;
    amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,
    wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,
    ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
Usandipenyetsetse;
    pakuti maso ako amanditenga mtima.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
    zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa
    zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,
iliyonse ili ndi ana amapasa,
    palibe imene ili yokha.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,
    masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,
    ndi azikazi 80,
    ndi anamwali osawerengeka;
koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;
    mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,
    mwana wapamtima wa amene anamubereka.
Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;
    akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,
    wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,
    wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi
    kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,
kukaona ngati mpesa waphukira
    kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Ndisanazindikire kanthu,
    ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;
    bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,
    pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola
    mu nsapato wavalazo!
Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,
    ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino
    chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.
Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu
    utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,
    ngati mphoyo zamapasa.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.
Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,
    amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.
Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,
    yoyangʼana ku Damasiko.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.
    Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;
    mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,
    iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,
    ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;
    ndidzathyola zipatso zake.”
Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,
    fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
    ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,
    ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 Wokondedwayo ine ndine wake,
    ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,
    tikagone ku midzi.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,
    tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,
ngati maluwa ake ayamba kuoneka,
    komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.
    Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,
    ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,
zatsopano ndi zakale zomwe,
    zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,
    amene anayamwa mawere a amayi anga!
Ndikanakumana nawe pa njira,
    ndikanakupsompsona,
    ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
Ndikanakutenga
    ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,
    amayi amene anandiphunzitsa,
ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,
    zotsekemera za makangadza.
Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere
    ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:
    musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa
    mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,
    atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,
    pamenepo ndi pamene amayi anachirira,
    pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
Undiyike pamtima pako ngati chidindo,
    ngati chidindo cha pa dzanja lako;
pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,
    nsanje ndiyaliwuma ngati manda.
Chikondi chimachita kuti lawilawi
    ngati malawi a moto wamphamvu.
Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,
    mitsinje singachikokolole chikondicho.
Ngati wina apereka chuma chonse
    cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,
    adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,
    koma alibe mawere,
kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu
    pa tsiku limene adzamufunsire?
Ngati iye ndi khoma,
    tidzamumangira nsanja ya siliva.
Ngati iye ndi chitseko,
    tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10 Ine ndili ngati khoma,
    ndipo mawere anga ndi nsanja zake.
Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa
    ndine wobweretsa mtendere.
11 Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;
    iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,
aliyense mwa iwo ankayenera kupereka
    ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
12 Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.
    Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000
    ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13 Iwe amene umakhala mʼminda
    uli pamodzi ndi anzako,
    ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14 Fulumira wokondedwa wanga,
    ndipo ukhale ngati gwape
kapena mwana wa mbawala
    wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

Agalatiya 4

Chimene ndikunena ndi chakuti, ngati mlowamʼmalo akali wamngʼono, sasiyana ndi kapolo, ngakhale kuti chuma chonse ndi chake. Mwanayo ayenera kumvera omulera ndiponso anthu oyangʼanira chuma mpaka nthawi imene abambo ake anakhazikitsa. Chomwechonso, ife pamene tinali ana, tinali akapolo a miyambo ya dziko lapansi. Koma nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake, wobadwa mwa mayi, wobadwa pansi pa lamulo, kudzawombola amene anali pansi pa lamulo, kuti tilandiridwe monga ana. Ndipo popeza ndinu ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake kuti alowe mʼmitima mwathu, Mzimu amene amafuwula kuti, “Abba, Atate.” Choncho sindiwenso kapolo, koma mwana wa Mulungu. Tsono popeza ndiwe mwana wake, Mulungu wakusandutsanso mlowamʼmalo.

Nkhawa ya Paulo chifukwa cha Agalatiya

Koma poyamba pamene simunkamudziwa Mulungu, munali akapolo a zimene mwachilengedwe si milungu. Koma tsopano pakuti mukumudziwa Mulungu, kapena ndinene kuti Mulungu akukudziwani, nʼchifukwa chiyani mukubwereranso ku miyambo yofowoka ndi yomvetsa chisoni? Kodi mukufuna musandukenso akapolo? 10 Mumasunga masiku, miyezi ndi nyengo ndi zaka. 11 Ine ndikuopa kuti mwina ntchito zanga pa inu ndinagwira pachabe.

12 Abale, ndikukudandaulirani, mukhale ngati ine, popeza ine ndinakhala ngati inu. Inu simunandilakwire. 13 Monga inu mukudziwa ndinkakulalikirani Uthenga Wabwino ndili wofowoka. 14 Ngakhale kuti matendawo anali ngati mayesero kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane. Komatu inu munandilandira ngati kuti ndinali mngelo wa Mulungu, ngati kuti ndinali Khristu Yesu mwini. 15 Kodi chimwemwe chanu chonse chija chili kuti? Ine nditha kuchitira umboni kuti, ngati kukanatheka, inu mukanakolowola maso anu ndi kundipatsa. 16 Kodi tsopano ine ndasanduka mdani wanu chifukwa ndakuwuzani choonadi?

17 Anthu amenewo akuchita changu kuti akukopeni, koma changu chawocho sichabwino. Chimene iwo akufuna ndi chakuti akuchotseni inu kwa ife, kuti mukachite changu powathandiza iwowo. 18 Nʼkwabwino kuchita changu, ngati cholingacho chili chabwino ndi kukhala otero nthawi zonse osati pokhapo pamene ine ndili ndi inu. 19 Ana anga okondedwa, inu amene ine ndikukumveraninso zowawa za kubereka kufikira Khristu atawumbidwa mwa inu, 20 ine ndikanakonda ndikanakhala nanu tsopano kuti ndisinthe mawu anga, chifukwa ndathedwa nanu nzeru.

Hagara ndi Sara

21 Tandiwuzani, inu, abale amene mukufuna kukhala pansi pa lamulo, kodi simukudziwa chimene lamulo limanena? 22 Pakuti zinalembedwa kuti Abrahamu anali ndi ana aamuna awiri, wina mayi wake anali kapolo ndipo wina mayi wake anali mfulu. 23 Mwana wake wobadwa mwa kapolo anabadwa mwathupi; koma mwana wake wobadwa mwa mfulu anabadwa monga mwa lonjezo.

24 Zinthu izi zinali ngati fanizo, pakuti amayi awiriwa akuyimira mapangano awiri. Pangano limodzi ndi lochokera mʼPhiri la Sinai, ndiye Hagara, ndipo amabereka ana amene ndi akapolo. 25 Tsono Hagara, akuyimira Phiri la Sinai ku Arabiya amene afanizidwa ndi mzinda wa Yerusalemu wa lero, chifukwa ali mu ukapolo pamodzi ndi ana ake. 26 Koma Yerusalemu wakumwamba ndiye mfulu, ndipo ndiye mayi wathu. 27 Pakuti kwalembedwa kuti,

“Sangalala, iwe mayi wosabala,
    amene sunabalepo mwana;
imba nthungululu ndi kufuwula mwachimwemwe,
    iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
    kuposa mkazi wokwatiwa.”

28 Tsono inu abale, ndinu ana alonjezo ngati Isake. 29 Nthawi imeneyo mwana wobadwa mwathupi anazunza mwana wobadwa mwamphamvu za Mzimu. Zili chimodzimodzinso lero. 30 Kodi Malemba akuti chiyani? “Muchotse kapoloyo pamodzi ndi mwana wake, chifukwa mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wamfulu.” 31 Chifukwa chake, abale, ife sindife ana akapolo, koma ana a mfulu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.