Old/New Testament
Mwamuna
4 Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!
Ndithudi, ndiwe wokongola!
Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,
zochokera kozisambitsa kumene.
Iliyonse ili ndi ana amapasa;
palibe imene ili yokha.
3 Milomo yako ili ngati mbota yofiira;
pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba
kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,
yomangidwa bwino ndi yosalala;
pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,
zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,
ngati ana amapasa a nswala
amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira
ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,
ndidzapita ku phiri la mure
ndi ku chitunda cha lubani.
7 Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;
palibe chilema pa iwe.
8 Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,
tiye tichoke ku Lebanoni,
utsikepo pa msonga ya Amana,
kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,
kuchoka ku mapanga a mikango
ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
9 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,
iwe wanditenga mtima
ndi kapenyedwe ka maso ako,
ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!
Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,
ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;
pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.
Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;
ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;
muli zipatso zokoma kwambiri,
muli hena ndi nadi,
14 nadi ndi safiro,
kalamusi ndi sinamoni,
komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.
Mulinso mure ndi aloe
ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,
chitsime cha madzi oyenda,
mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
Mkazi
16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,
ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!
Uzira pa munda wanga,
kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.
Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake
ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.
Mwamuna
5 Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;
ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.
Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;
ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.
Abwenzi
Idyani abwenzi anga, imwani;
Inu okondana, imwani kwambiri.
Mkazi
2 Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.
Tamverani, bwenzi langa akugogoda:
“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,
nkhunda yanga, wangwiro wanga.
Mutu wanga wanyowa ndi mame,
tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 Ndavula kale zovala zanga,
kodi ndizivalenso?
Ndasamba kale mapazi anga
kodi ndiwadetsenso?
4 Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;
mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,
ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,
zala zanga zinali mure chuchuchu,
pa zogwirira za chotsekera.
6 Ndinamutsekulira wachikondi wanga,
koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.
Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.
Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.
Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 Alonda anandipeza
pamene ankayendera mzindawo.
Anandimenya ndipo anandipweteka;
iwo anandilanda mwinjiro wanga,
alonda a pa khoma aja!
8 Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,
mukapeza wokondedwa wangayo,
kodi mudzamuwuza chiyani?
Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
Abwenzi
9 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?
Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani
kuti uzichita kutipempha motere?
Mkazi
10 Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi
pakati pa anthu 1,000.
11 Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;
tsitsi lake ndi lopotanapotana,
ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 Maso ake ali ngati nkhunda
mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,
zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya
zopatsa fungo lokoma.
Milomo yake ili ngati maluwa okongola
amene akuchucha mure.
14 Manja ake ali ngati ndodo zagolide
zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.
Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu
woyikamo miyala ya safiro.
15 Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,
yokhazikika pa maziko a golide.
Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,
abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;
munthuyo ndi wokongola kwambiri!
Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,
inu akazi a ku Yerusalemu.
Chikhulupiriro Kapena Ntchito za Lamulo
3 Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani? Tinamuonetsa poyera pamaso panu Yesu Khristu monga wopachikidwa pa mtanda. 2 Ine ndikufuna ndiphunzire kuchokera kwa inu chinthu chimodzi ichi: Kodi munalandira Mzimu pochita ntchito za lamulo, kapena pokhulupirira zimene munamva? 3 Kani ndinu opusa chotere? Inu mutayamba ndi Mzimu, kodi mukufuna kutsiriza ndi ntchito zathupi? 4 Kodi munavutika kwambiri pachabe, ngati kunali kwachabedi? 5 Kodi Mulungu amene anakupatsani Mzimu wake ndi kuchita zodabwitsa pakati panu, amachita zimenezi chifukwa mumachita ntchito za lamulo kapena chifukwa mumakhulupirira zimene munamva? 6 Nʼchimodzimodzinso Abrahamu, “Iye anakhulupirira Mulungu, ndipo Mulungu anamutenga kukhala wolungama.”
7 Tsono zindikirani kuti amene akhulupirira, ndi ana a Abrahamu. 8 Malemba anaonetseratu kuti Mulungu adzalungamitsa anthu a mitundu ina mwachikhulupiriro, ndipo ananeneratu Uthenga Wabwino kwa Abrahamu kuti, “Mitundu yonse ya anthu idzadalitsika kudzera mwa iwe.” 9 Choncho iwo amene ali ndi chikhulupiriro ndi odalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu, munthu wachikhulupiriro.
10 Onse amene amadalira ntchito za lamulo ndi otembereredwa, pakuti zalembedwa mʼBuku la Malamulo kuti, “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita zonse zimene zalembedwa mʼBuku la Malamulo.” 11 Chodziwikiratu nʼchakuti palibe amene amalungamitsidwa pamaso pa Mulungu ndi lamulo, chifukwa, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.” 12 Koma chikhulupiriro si Malamulo, chifukwa Malemba akuti, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” 13 Khristu anatiwombola ku temberero la lamulo pokhala temberero mʼmalo mwathu, pakuti analemba kuti, “Aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa.” 14 Iye anatiwombola ife ndi cholinga chakuti madalitso woperekedwa kwa Abrahamu abwere kwa anthu a mitundu ina kudzera mwa Khristu Yesu, kuti ndi chikhulupiriro tilandire lonjezo la Mzimu.
Lamulo ndi Lonjezo
15 Abale, ndiloleni ndipereke chitsanzo cha zochitika mʼmoyo wa tsiku ndi tsiku. Pangano likakhazikitsidwa palibe amene angachotsepo kapena kuwonjezerapo, choncho ndi chimodzimodzi pa nkhani iyi. 16 Malonjezo awa anaperekedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbewu yake. Malemba sakunena kuti, “kwa mbewu zake,” kutanthauza anthu ambiri, koma, “kwa mbewu yako,” kutanthauza munthu mmodzi, amene ndi Khristu. 17 Chimene ndikutanthauza ine ndi ichi: Malamulo amene anabwera patatha zaka 430, sangathetse pangano limene linakhazikitsidwa kale ndi Mulungu ndi kuliwononga lonjezolo. 18 Ngati madalitso athu akudalira ntchito za lamulo ndiye kuti madalitsowo sakupatsidwa chifukwa cha lonjezo. Koma Mulungu mwachisomo chake anadalitsa Abrahamu kudzera mu lonjezo.
19 Nanga tsono cholinga cha lamulo chinali chiyani? Linaperekedwa chifukwa cha zolakwa mpaka itafika mbewu imene lonjezo limanena. Malamulowo anaperekedwa ndi angelo kudzera mwa mʼkhalapakati. 20 Ngakhale zili chomwecho, mʼkhalapakati sayimira mbali imodzi yokha, koma Mulungu ndi mmodzi.
21 Kodi ndiye kuti lamulo limatsutsana ndi malonjezo a Mulungu? Ayi. Nʼkosatheka! Pakuti ngati tikanapatsidwa malamulo opatsa moyo ndiye kuti mwa lamulo tikanakhala olungama. 22 Koma Malemba akunenetsa kuti dziko lonse lili mu ulamuliro wauchimo, kuti mwachikhulupiriro mwa Yesu Khristu, chimene chinalonjezedwa chiperekedwe kwa amene akhulupirira.
23 Chikhulupiriro ichi chisanabwere, ife tinali mʼndende ya lamulo, otsekeredwa mpaka pamene chikhulupiriro chikanavumbulutsidwa. 24 Choncho lamulo linayikidwa kukhala lotiyangʼanira kuti lititsogolere kwa Khristu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro. 25 Tsopano pakuti chikhulupiriro chabwera, ife sitilinso mu ulamuliro wa lamulo.
Ana a Mulungu
26 Nonse ndinu ana a Mulungu kudzera mʼchikhulupiriro mwa Khristu Yesu, 27 pakuti nonse amene munalumikizana ndi Khristu mu ubatizo munavala Khristu. 28 Palibe Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu, mwamuna kapena mkazi, pakuti nonse ndinu amodzi mwa Khristu Yesu. 29 Ngati inu muli ake a Khristu, ndiye kuti ndinu mbewu ya Abrahamu, ndi olowamʼmalo molingana ndi lonjezo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.