Old/New Testament
Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno
4 Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:
ndinaona misozi ya anthu opsinjika,
ndipo iwo alibe owatonthoza;
mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo
ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 Ndipo ndinanena kuti akufa,
amene anafa kale,
ndi osangalala kuposa amoyo,
amene akanalibe ndi moyo.
3 Koma wopambana onsewa
ndi amene sanabadwe,
amene sanaone zoyipa
zimene chimachitika pansi pano.
4 Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 Chitsiru chimangoti manja ake lobodo
ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,
kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,
ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Panali munthu amene anali yekhayekha;
analibe mwana kapena mʼbale.
Ntchito yake yolemetsa sinkatha,
ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.
Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?
Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”
Izinso ndi zopandapake,
zosasangalatsa!
9 Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,
chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 Ngati winayo agwa,
mnzakeyo adzamudzutsa.
Koma tsoka kwa munthu amene agwa
ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.
Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,
koma anthu awiri akhoza kudziteteza.
Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
Kutukuka Nʼkopandapake
13 Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14 Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15 Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16 Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.
Lemekeza Mulungu
5 Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.
2 Usamafulumire kuyankhula,
usafulumire mu mtima mwako
kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.
Mulungu ali kumwamba
ndipo iwe uli pa dziko lapansi,
choncho mawu ako akhale ochepa.
3 Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,
ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.
4 Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. 5 Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. 6 Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? 7 Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.
Chuma Nʼchopandapake
8 Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. 9 Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.
10 Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;
aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.
Izinso ndi zopandapake.
11 Chuma chikachuluka
akudya nawo chumacho amachulukanso.
Nanga mwini wake amapindulapo chiyani
kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?
12 Wantchito amagona tulo tabwino
ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,
koma munthu wolemera, chuma
sichimulola kuti agone.
13 Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:
chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,
14 kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,
kotero kuti pamene wabereka mwana
alibe kanthu koti amusiyire.
15 Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,
ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.
Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta
palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.
16 Izinso ndi zoyipa kwambiri:
munthu adzapita monga momwe anabwerera,
ndipo iye amapindula chiyani,
pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?
17 Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,
kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.
18 Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19 Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20 Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.
6 Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri: 2 Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.
3 Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo. 4 Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika. 5 Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja, 6 ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?
7 Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake,
komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
8 Kodi munthu wanzeru
amaposa motani chitsiru?
Kodi munthu wosauka amapindula chiyani
podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
9 Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso
kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima.
Izinso ndi zopandapake,
nʼkungodzivuta chabe.
10 Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina,
za mmene munthu alili nʼzodziwika;
sangathe kutsutsana ndi munthu
amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
11 Mawu akachuluka
zopandapake zimachulukanso,
nanga munthu zimamupindulira chiyani?
12 Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?
Masomphenya a Paulo ndi Minga ya Mʼthupi Mwake
12 Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye. 2 Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 3 Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 4 Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena. 5 Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga. 6 Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula, 7 kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza. 8 Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere. 9 Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine. 10 Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.
Paulo Akhudzidwa ndi Akorinto
11 Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja. 12 Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu. 13 Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!
14 Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana. 15 Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono? 16 Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani. 17 Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu? 18 Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?
19 Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani. 20 Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo. 21 Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.