Old/New Testament
Phindu Lina la Nzeru
3 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga,
mtima wako usunge malamulo anga.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka
ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere.
Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda
ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino
pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse
ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,
ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Usamadzione ngati wa nzeru.
Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino
ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse;
zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri,
ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova,
ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda,
monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru,
munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva,
phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali;
ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali;
mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa,
ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa;
wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru.
Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka
ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino.
Zimenezi zisakuchokere.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo,
moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu,
ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha;
ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi
kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima
ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino,
pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti,
“Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa”
pamene uli nazo tsopano.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako,
amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa
pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa
kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa
koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa,
koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza,
koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu,
koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Nzeru Iposa Zonse
4 Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
Choncho musasiye malangizo anga.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
“Ugwiritse mawu anga pa mtima pako,
usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;
idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa
kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
tchera khutu ku mawu anga.
21 Usayiwale malangizo angawa,
koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo;
uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;
usapite kumene kuli zoyipa.
Chenjezo kwa Mkazi Wachigololo
5 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi,
tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru
ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi.
Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu;
ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa;
akamayenda ndiye kuti akupita ku manda.
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo;
njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Tsopano ana inu, mundimvere;
musawasiye mawu anga.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo,
usayandikire khomo la nyumba yake,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena;
ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako
ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula,
thupi lako lonse litatheratu.
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo!
Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 Sindinamvere aphunzitsi anga
kapena alangizi anga.
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke
pakati pa msonkhano wonse.”
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako,
madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu?
Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha,
osati uyigawireko alendo.
18 Yehova adalitse kasupe wako,
ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino.
Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse,
ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo?
Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona,
ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha;
zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo,
adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo,
Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
2 Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
Mulungu Mwini Chitonthozo
3 Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse. 4 Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu. 5 Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri. 6 Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife. 7 Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
8 Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo. 9 Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa. 10 Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe. 11 Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
Paulo Afotokoza za Kusintha kwa Ulendo Wake
12 Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu. 13 Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa. 14 Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.
15 Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri. 16 Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya. 17 Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”
18 Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.” 19 Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.” 20 Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu. 21 Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife, 22 nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
23 Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni. 24 Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.