Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 143-145

Salimo la Davide.

143 Yehova imvani pemphero langa,
    mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;
mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu
    bwerani kudzandithandiza.
Musazenge mlandu mtumiki wanu,
    pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

Mdani akundithamangitsa,
    iye wandipondereza pansi;
wachititsa kuti ndikhale mu mdima
    ngati munthu amene anafa kale.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;
    mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

Ndimakumbukira masiku amakedzana;
    ndimalingalira za ntchito yanu yonse,
    ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;
    moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.
            Sela

Yehova ndiyankheni msanga;
    mzimu wanga ukufowoka.
Musandibisire nkhope yanu,
    mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,
    pakuti ine ndimadalira Inu.
Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,
    pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,
    pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,
    popeza ndinu Mulungu wanga;
Mzimu wanu wabwino unditsogolere
    pa njira yanu yosalala.

11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;
    mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;
    wonongani adani anga,
    pakuti ndine mtumiki wanu.

Salimo la Davide.

144 Atamandike Yehova Thanthwe langa,
    amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
    zala zanga kumenya nkhondo.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,
    linga langa ndi mpulumutsi wanga,
chishango changa mmene ine ndimathawiramo,
    amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,
    mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Munthu ali ngati mpweya;
    masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;
    khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;
    ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;
    landitseni ndi kundipulumutsa,
ku madzi amphamvu,
    mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,
    amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;
    ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,
    amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11 Landitseni ndi kundipulumutsa,
    mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,
    amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo
    adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,
ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala
    zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza
    ndi zokolola za mtundu uliwonse.
Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda
    pa mabusa athu.
14     Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.
Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,
    sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,
    mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;
    odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Salimo la matamando la Davide.

145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
    ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
    ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
    ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
    Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
    ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
    ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
    ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
    wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yehova ndi wabwino kwa onse;
    amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
    oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
    ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
    ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
    ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
    ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
    ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
    ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
    ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
    ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
    onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
    amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
    koma adzawononga anthu onse oyipa.

21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
    Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
    ku nthawi za nthawi.

1 Akorinto 14:21-40

21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti,

“Ndidzayankhula kwa anthu awa,
    kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo
ndiponso ndi milomo yachilendo.
    Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine,
            akutero Ambuye.”

22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira. 23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala? 24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse 25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”

Kupembedza Mwadongosolo

26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo. 27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo. 28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.

29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo. 30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete. 31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa. 32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri. 33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.

Amayi Akhale Chete mu Mpingo

34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera. 35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.

36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha? 37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye. 38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.

39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime. 40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.