Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 91-93

91 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba
    adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,
    Mulungu wanga amene ndimadalira.”

Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje
    ndi ku mliri woopsa;
Adzakuphimba ndi nthenga zake,
    ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;
    kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,
    kapena muvi wowuluka masana,
kapena mliri umene umayenda mu mdima,
    kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,
    anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,
    koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Udzapenya ndi maso ako
    ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;
    wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,
    zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,
    kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo,
    kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka,
    udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;
    ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;
    ndidzakhala naye pa mavuto,
    ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali
    ndi kumupulumutsa.”

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

92 Nʼkwabwino kutamanda Yehova
    ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
Kulengeza chikondi chanu mmawa,
    ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi
    ndi mayimbidwe abwino a zeze.

Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;
    Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,
    maganizo anu ndi ozamadi!
Munthu wopanda nzeru sadziwa,
    zitsiru sizizindikira,
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu
    ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,
adzawonongedwa kwamuyaya.

Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

Zoonadi adani anu Yehova,
    zoonadi adani anu adzawonongeka;
    onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;
    mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,
    makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,
    adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,
    adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,
    adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;
    Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
93 Yehova akulamulira, wavala ulemerero;
    Yehova wavala ulemerero ndipo wadzimangirira mphamvu,
    dziko lonse lakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
Mpando wanu waufumu unakhazikika kalekale;
    Inu ndinu wamuyaya.

Nyanja zakweza Inu Yehova,
    nyanja zakweza mawu ake;
    nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.
Yehova ndi wamphamvu kupambana mkokomo wa madzi ambiri,
    ndi wamphamvu kupambana mafunde a nyanja,
    Yehova mmwamba ndi wamphamvu.

Malamulo anu Yehova ndi osasinthika;
    chiyero chimakongoletsa nyumba yanu
    mpaka muyaya.

Aroma 15:1-13

15 Ife amene tili ndi chikhulupiriro champhamvu tiziwalezera mtima anthu ofowoka, ndipo tisamadzikondweretse tokha. Aliyense wa ife akondweretse mnzake pomuchitira zabwino zomulimbikitsa. Pakuti ngakhale Khristu sanadzikondweretsa yekha koma, monga kwalembedwa kuti, “Chipongwe cha anthu okunyozani chinagwera Ine.” Pakuti zilizonse zimene zinalembedwa kale zinalembedwa kuti zitiphunzitse ife. Malembawo amatilimbikitsa kupirira kuti tikhale ndi chiyembekezo.

Mulungu amene amapereka kupirira ndi chilimbikitso akupatseni maganizo amodzi pakati panu monga inu mukutsatira Khristu Yesu, kotero kuti ndi mtima umodzi ndi movomerezana mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.

Tsopano landiranani wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, ndi cholinga choti Mulungu alemekezeke. Chifukwa kunena zoona, Khristu wasanduka mtumiki wa Ayuda, kuonetsa kuti Mulungu ndi wokhulupirika pa malonjezo amene anachita kwa makolo awo kuti a mitundu ina atamande Mulungu chifukwa cha chifundo chake. Monga kwalembedwa kuti,

“Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa a mitundu;
    ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”

10 Akutinso,

“Kondwerani inu anthu a mitundu ina pamodzi ndi anthu ake.”

11 Ndipo akutinso,

“Tamandani Ambuye, inu nonse a mitundu ina,
    ndi kuyimba zotamanda Iye, inu anthu onse.”

12 Ndiponso Yesaya akuti,

“Muzu wa Yese udzaphuka,
    wina amene adzauka kulamulira anthu a mitundu ina;
mwa Iye mudzakhala chiyembekezo cha a mitundu ina.”

13 Mulungu amene amatipatsa chiyembekezo adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pamene mukumudalira Iye, kuti chiyembekezo chanu chisefukire mwamphamvu ya Mzimu Woyera.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.