Old/New Testament
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Gititi. Salimo la ana a Kora.
84 Malo anu okhalamo ndi okomadi,
Inu Yehova Wamphamvuzonse!
2 Moyo wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka,
kufuna mabwalo a Yehova;
Mtima wanga ndi thupi langa zikufuwulira
Mulungu wamoyo.
3 Ngakhale timba wapeza nyumba yokhalamo,
ndiponso namzeze wadzipezera yekha chisa,
kumene amagonekako ana ake
pafupi ndi guwa lanu la nsembe,
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga.
4 Odala amene amakhala mʼNyumba yanu;
nthawi zonse amakutamandani.
Sela
5 Odala amene mphamvu yawo ili mwa Inu,
mitima yawo ikufunitsitsa kuyenda mʼmisewu yopita ku Ziyoni.
6 Pamene akudutsa chigwa cha Baka,
amachisandutsa malo a akasupe;
mvula ya chizimalupsa imadzazanso mayiwe ake.
7 Iwo amanka nakulirakulira mphamvu
mpaka aliyense ataonekera pamaso pa Mulungu mu Ziyoni.
8 Imvani pemphero langa, Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse;
mvereni Inu Mulungu wa Yakobo.
Sela
9 Yangʼanani chishango chathu, Inu Mulungu;
yangʼanani mokoma mtima pa wodzozedwa wanu.
10 Nʼkwabwino kukhala mʼmabwalo anu tsiku limodzi
kuposa kukhala kwina kwake kwa zaka 1,000;
Ine ndingakonde kukhala mlonda wa pa khomo la Nyumba ya Mulungu wanga
kuposa kukhala mʼmatenti a anthu oyipa.
11 Pakuti Yehova Mulungu ndi dzuwa ndi chishango;
Yehova amapereka chisomo ndi ulemu;
Iye sawamana zinthu zabwino
iwo amene amayenda mwangwiro.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse,
wodala ndi munthu amene amakhulupirira Inu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.
85 Yehova munakomera mtima dziko lanu;
munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu
ndi kuphimba machimo awo onse.
Sela
3 Munayika pambali ukali wanu wonse
ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso,
kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,
ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;
Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake,
koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,
kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;
chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,
ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,
ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Wolungama amapita patsogolo pake
ndi kukonza njira za mapazi ake.
Pemphero la Davide.
86 Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,
pakuti ndine wosauka ndi wosowa.
2 Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.
Inu ndinu Mulungu wanga;
pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu.
Inu ndinu Mulungu wanga.
3 Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,
pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.
4 Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,
pakuti ndimadalira Inu.
5 Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,
wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.
6 Yehova imvani pemphero langa;
mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.
7 Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,
pakuti Inu mudzandiyankha.
8 Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;
palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.
9 Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga
idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye;
iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.
10 Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;
Inu nokha ndiye Mulungu.
11 Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,
ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu;
patseni mtima wosagawikana
kuti ndilemekeze dzina lanu.
12 Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;
ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.
13 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;
mwandipulumutsa ku malo ozama a manda.
14 Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;
anthu ankhanza akufuna kundipha,
amene salabadira za Inu.
15 Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,
wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;
perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu
ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.
17 Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu
kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,
pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.
Nsembe za Moyo
12 Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu. 2 Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro.
3 Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani. 4 Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana. 5 Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake. 6 Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake. 7 Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse. 8 Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
Chikondi
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20 Koma,
“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.
Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.
Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.