Old/New Testament
Salimo la Solomoni.
72 Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,
Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,
anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,
timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu
ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;
adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,
nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa
ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;
chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina
ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake
ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali
adzabweretsa mitulo kwa iye,
mafumu a ku Seba ndi Seba
adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Mafumu onse adzamuweramira
ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,
wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa
ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa
pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 Iye akhale ndi moyo wautali;
golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye.
Anthu amupempherere nthawi zonse
ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;
pamwamba pa mapiri pakhale tirigu.
Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni;
zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya,
lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa.
Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye
ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli
amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya
dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.
Ameni ndi Ameni.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
BUKU LACHITATU
Masalimo 73–89
Salimo la Asafu.
73 Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,
kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;
ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,
pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Iwo alibe zosautsa;
matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 Saona mavuto monga anthu ena;
sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;
amadziveka chiwawa.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;
zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;
mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba
ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo
ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?
Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili;
nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;
pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto;
ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”
ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,
zinandisautsa kwambiri
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;
pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;
Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,
amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Monga loto pamene wina adzuka,
kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,
mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa
ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa;
ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;
mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu
ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?
Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,
koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga
ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;
Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.
Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga
ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
Chisankho Chopambana cha Mulungu
9 Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni. 2 Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga. 3 Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga, 4 anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake. 5 Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni.
6 Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli. 7 Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 8 Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu. 9 Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”
10 Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake. 11 Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire, 12 osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.” 13 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”
14 Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe! 15 Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti,
“Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo,
ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.