Old/New Testament
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.
60 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.
Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,
konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;
inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera
kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,
kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu
ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira,
pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,
pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?
Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife
ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,
pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano
ndipo tidzapondaponda adani athu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.
61 Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;
mvetserani pemphero langa.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu
ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;
tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,
nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya
ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;
mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,
zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;
ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu
ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.
62 Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;
chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?
Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,
ngati mpanda wogwedezeka?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa
kuti achoke pa malo ake apamwamba.
Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.
Ndi pakamwa pawo amadalitsa
koma mʼmitima yawo amatemberera.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;
chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:
Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;
khuthulani mitima yanu kwa Iye,
pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.
Sela
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe;
anthu apamwamba ndi bodza chabe;
ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;
iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Musadalire kulanda mwachinyengo
kapena katundu wobedwa;
ngakhale chuma chanu chichuluke,
musayike mtima wanu pa icho.
11 Mulungu wayankhula kamodzi,
ine ndamvapo zinthu ziwiri;
choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.
Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu
molingana ndi ntchito zake.
Mtendere ndi Chimwemwe
5 Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2 Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3 Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4 Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5 Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
6 Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7 Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8 Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
9 Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu
12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.