Old/New Testament
33 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,
nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe;
muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano;
imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;
Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;
dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,
zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;
amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova;
anthu onse amulemekeze Iye.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;
Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;
Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,
zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,
anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi
ndi kuona anthu onse;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira
onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse,
amaona zonse zimene akuchita.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;
palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,
ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;
amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 kuwawombola iwo ku imfa
ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;
Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera,
pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Chikondi chanu chosatha
chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.
34 Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;
matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova;
anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;
tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;
anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;
nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;
Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye
ndi kuwalanditsa.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;
wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake,
pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala
koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Bwerani ana anga, mundimvere;
ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake
ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 asunge lilime lake ku zoyipa
ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Maso a Yehova ali pa olungama
ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,
kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;
Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima
ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,
Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Iye amateteza mafupa ake onse,
palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa;
adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Yehova amawombola atumiki ake;
aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Felike Amva Mlandu wa Paulo
24 Patapita masiku asanu mkulu wa ansembe Hananiya, pamodzi ndi akuluakulu ena ndi katswiri woyankhulira anthu pa milandu wotchedwa Tertuliyo anapita ku Kaisareya ndipo anafotokoza mlandu wa Paulo kwa Bwanamkubwayo. 2 Atamuyitana Paulo, ndipo Tertuliyo anafotokozera Felike nkhani yonse ya Paulo. Iye anati, “Wolemekezeka, ife takhala pamtendere nthawi yayitali chifukwa cha inu, ndipo utsogoleri wanu wanzeru wabweretsa kusintha mʼdziko lino. 3 Wolemekezeka Felike ife timazilandira zimenezi moyamika kwambiri ponseponse ndi mwa njira iliyonse. 4 Koma kuti tisakuchedwetseni, ndikupempha kuti mwa kuleza mtima kwanu mutimvere ife.
5 “Ife tapeza kuti munthu uyu amayambitsa mavuto ndi kuwutsa mapokoso pakati pa Ayuda onse a dziko lonse lapansi. Iyeyu ndi mtsogoleri wa mpatuko wa Anazareti. 6 Anayesera ngakhale kudetsa Nyumba ya Mulungu wathu. Ndiye ife tinamugwira. 7 Koma, mkulu wa asilikali Lusiya anafika mwamphamvu namuchotsa mʼmanja mwathu. 8 Ndipo Lusiya analamula kuti amene anali naye ndi mlandu abwere kwa inu. Mukamufunsa ameneyu kwa nokha mudzadziwa choonadi cha zimene ife tikumunenera.”
9 Ayuda anavomereza nanenetsa kuti zimenezi zinali zoona.
10 Bwanamkubwayo atakodola Paulo ndi kulola kuti ayankhule, Pauloyo anati, “Ine ndikudziwa kuti inu mwakhala mukuweruza dziko lino zaka zambiri, kotero ndikukondwera kuti ndikudziteteza ndekha pamaso panu. 11 Inu mukhoza kupeza umboni wake. Sipanapite masiku khumi ndi awiri chipitireni changa ku Yerusalemu kukapembedza. 12 Amene akundiyimba mlanduwa sanandipeze mʼNyumba ya Mulungu ndi kutsutsana ndi wina aliyense kapena kuyambitsa chisokonezo mʼsunagoge kapena pena paliponse mu mzindamo. 13 Ndipo sangathe kupereka umboni wa mlandu umene akundiyimba inewu. 14 Komatu ine ndikuvomera kuti ndimapembedza Mulungu wa makolo athu, monga wotsatira wa Njirayo, imene iwo akuyitchula mpatuko. Ine ndimakhulupirira chilichonse chimene chimagwirizana ndi malamulo ndiponso zimene zinalembedwa ndi Aneneri. 15 Ine ndili nacho chiyembekezo chomwecho chimene iwo ali nacho mwa Mulungu, kuti kudzakhala kuuka kwa akufa kwa olungama ndiponso kwa ochimwa. 16 Kotero ine ndimayesetsa kuti ndikhale ndi chikumbumtima chosanditsutsa pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
17 “Patapita zaka zambiri, ndinabwera ku Yerusalemu kudzapereka mphatso kwa anthu osauka a mtundu wanga komanso kudzapereka nsembe. 18 Pamene ndinkachita zimenezi, iwo anandipeza mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nditachita mwambo wodziyeretsa. Panalibe gulu la anthu kapena kuti ndimachita za chisokonezo chilichonse. 19 Koma pali Ayuda ena ochokera ku Asiya, amene amayenera kukhala pano pamaso panu, kundiyimba mlandu ngati ali ndi kalikonse konditsutsa ine. 20 Kapena awa amene ali panowa anene mlandu umene anapeza mwa ine, pamene ndinayima pamaso pa Bwalo lawo Lalikulu. 21 Koma cholakwa changa chingathe kukhala chokhachi chakuti, nditayima pamaso pawo ndinafuwula kuti, ‘Mukundiweruza ine lero chifukwa ndimakhulupirira kuti akufa adzauka.’ ”
22 Kenaka Felike, amene amadziwa bwino za Njirayo, anayamba wayimitsa mlanduwo, nati, “Ndidzagamula mlandu wako akabwera mkulu wa asilikali Lusiya.” 23 Iye analamulira woyangʼanira asilikali 100 kuti alondere Paulo, koma azimupatsako ufulu ndiponso kulola abwenzi ake kuti adzimusamalira.
24 Patapita masiku angapo Felike anabwera pamodzi ndi mkazi wake Drusila, amene anali Myuda. Anayitana Paulo ndipo anamvetsera zimene amayankhula za chikhulupiriro mwa Khristu Yesu. 25 Paulo atayankhula za chilungamo, za kudziretsa ndiponso za chiweruzo chimene chikubwera, Felike anachita mantha ndipo anati, “Basi tsopano! Pita. Tidzakuyitanitsa tikadzapeza mpata.” 26 Pa nthawi imeneyi amayembekeza kuti Paulo adzamupatsa ndalama, nʼchifukwa chake amamuyitanitsa kawirikawiri ndi kumayankhula naye.
27 Patapita zaka ziwiri, Porkiyo Festo analowa mʼmalo mwa Felike, koma anamusiya Paulo mʼndende, chifukwa amafuna kuti Ayuda amukonde.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.