Old/New Testament
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.
7 Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 mwina angandikadzule ngati mkango,
ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Inu Yehova Mulungu wanga,
ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
ndipo mundigoneke pa fumbi.
Sela
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
Alamulireni muli kumwambako;
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Inu Mulungu wolungama,
amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
Mulungu adzanola lupanga lake,
Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide.
8 Inu Yehova Ambuye athu,
dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu
mʼmayiko onse akumwamba.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda,
Inu mwakhazikitsa mphamvu
chifukwa cha adani anu,
kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba,
ntchito ya zala zanu,
mwezi ndi nyenyezi,
zimene mwaziyika pa malo ake,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira,
ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba
ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu;
munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi
ndi nyama zakuthengo,
8 mbalame zamlengalenga
ndi nsomba zamʼnyanja
zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 Inu Yehova, Ambuye athu,
dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide.
9 Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse;
ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu;
Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Adani anga amathawa,
iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga;
Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa;
Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani,
mwafafaniza mizinda yawo;
ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya;
wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo;
adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima,
linga pa nthawi ya mavuto.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu,
pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni;
lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira;
Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira!
Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 kuti ndilengeze za matamando anu
pa zipata za ana aakazi a Ziyoni,
kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba;
mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake;
oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo.
Higayoni. Sela
17 Oyipa amabwerera ku manda,
mitundu yonse imene imayiwala Mulungu.
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse,
kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane;
mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova;
mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba.
Sela
Ku Korinto
18 Zitatha izi, Paulo anachoka ku Atene ndipo anapita ku Korinto. 2 Kumeneko anakumana ndi Myuda wina dzina lake Akula, nzika ya ku Ponto amene anali atangofika kumene kuchokera ku Italiya pamodzi ndi mkazi wake Prisila, chifukwa Klaudiyo analamula Ayuda onse kuti achoke ku Roma. Paulo anapita kukawaona. 3 Popeza Paulo anali mʼmisiri wosoka matenti monga iwo, iye anakhala nawo namagwirira ntchito pamodzi. 4 Tsiku la Sabata lililonse Paulo amakambirana ndi anthu mʼsunagoge, kufuna kukopa Ayuda ndi Agriki.
5 Sila ndi Timoteyo atafika kuchokera ku Makedoniya, Paulo ankangogwira ntchito yolalikira yokha basi, kuchitira umboni Ayuda kuti Yesu ndiye Khristu. 6 Koma pamene Ayuda anatsutsana naye ndi kumuchita chipongwe, iye anakutumula zovala zake nati, “Magazi anu akhale pamitu yanu! Ine ndilibe mlandu. Kuyambira tsopano ndipita kwa anthu a mitundu ina.”
7 Ndipo Paulo anatuluka mʼsunagoge napita ku nyumba yoyandikana ndi sunagoge ya Tito Yusto, munthu wopembedza Mulungu. 8 Krispo, mkulu wa sunagoge, pamodzi ndi a pa banja lake lonse anakhulupirira Ambuye; ndiponso Akorinto ambiri amene anamva Paulo akulalikira anakhulupiriranso nabatizidwa.
9 Usiku wina Ambuye anaonekera kwa Paulo mʼmasomphenya namuwuza kuti, “Usaope, pitiriza kuyankhula, usakhale chete. 10 Pakuti Ine ndili nawe, palibe aliyense amene adzakukhudza ndi kukuchitira choyipa, chifukwa mu mzinda muno ndili ndi anthu ambiri.” 11 Choncho Paulo anakhala kumeneko chaka ndi miyezi isanu ndi umodzi akuphunzitsa Mawu a Mulungu.
12 Galiyo ali mkulu wa boma wa ku Akaya, Ayuda mogwirizana anamugwira Paulo napita naye ku bwalo la milandu. 13 Iwo anati, “Munthu uyu akukopa anthu kuti azipembedza Mulungu mwanjira zotsutsana ndi malamulo athu.”
14 Pamene Paulo ankati ayankhule, Galiyo anati kwa Ayuda, “Ukanakhala mlandu wochita choyipa kapena wolakwira mnzake, bwenzi nditakumverani bwinobwino. 15 Koma popeza ndi nkhani yokhudza mawu, mayina ndi malamulo anu, kambiranani nokhanokha. Ine sindidzaweruza zinthu zimenezi.” 16 Kotero iye anawapirikitsa mʼbwalo la milandu. 17 Kenaka iwo anagwira Sositene, mkulu wa sunagoge, ndipo anamumenya mʼbwalo la milandu momwemo. Koma Galiyo sanasamale zimenezi.
Prisila, Akula ndi Apolo
18 Paulo anakhalabe ku Korinto masiku ambiri. Kenaka anawasiya abale nakwera sitima ya pamadzi kupita ku Siriya, pamodzi ndi Prisila ndi Akula. Asanakakwere sitima ya pamadzi, anameta tsitsi lake ku Kenkreya chifukwa anali atalumbira. 19 Iwo anafika ku Efeso, kumene Paulo anasiyako Prisila ndi Akula. Iye yekha analowa mʼsunagoge nakambirana ndi Ayuda. 20 Iwo atapempha kuti akakhale nawo nthawi yayitali, iye anakana. 21 Koma pamene amachoka anawalonjeza kuti, “Ndidzabweranso Mulungu akalola.” Ndipo anakwera sitima ya pamadzi kuchoka ku Efeso. 22 Pamene Paulo anafika ku Kaisareya, anakwera kukapereka moni ku mpingo kenaka anatsikira ku Antiokeya.
23 Atakhala kwa kanthawi ku Antiokeya, Paulo anachokako nayendera madera onse a ku Galatiya ndi ku Frugiya kulimbikitsa ophunzira onse.
Za Apolo
24 Pa nthawi yomweyi Myuda wina dzina lake Apolo, mbadwa ya ku Alekisandriya anafika ku Efeso. Anali munthu wophunzira ndi wodziwa bwino Malemba. 25 Apoloyu anaphunzitsidwa njira ya Ambuye, ndipo anayankhula ndi changu chachikulu naphunzitsa za Yesu molondola, ngakhale amadziwa ubatizo wa Yohane wokha. 26 Iye anayamba kuyankhula mʼsunagoge molimba mtima. Pamene Prisila ndi Akula anamva, iwo anamuyitanira ku nyumba yawo ndipo anamufotokozera njira ya Mulungu molongosoka bwino.
27 Pamene Apolo anafuna kupita ku Akaya, abale anamulimbikitsa, nalemba kalata kwa ophunzira a kumeneko kuti amulandire. Atafika kumeneko, anathandiza kwambiri amene anakhulupirira mwachisomo. 28 Pakuti iye anatsutsa Ayuda mwamphamvu pamaso pa anthu, natsimikiza kuchokera mʼMalemba kuti Yesu ndiye Khristu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.