Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yobu 17-19

17 “Mtima wanga wasweka,
    masiku anga atha,
    manda akundidikira.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira;
    maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.

“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna.
    Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu;
    choncho simudzawalola kuti apambane.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma,
    ana ake sadzaona mwayi.

“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense,
    munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni;
    ndawonda ndi mutu womwe.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi;
    anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo,
    ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.

10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo,
    sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka,
    pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana,
    nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda,
    ngati ndiyala bedi langa mu mdima,
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’
    ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti?
    Ndani angaone populumukira panga?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse,
    polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.”

Mawu a Bilidadi

18 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?
    Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe
    ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,
    kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?
    Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;
    malawi a moto wake sakuwalanso.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;
    nyale ya pambali pake yazima.
Mayendedwe ake amgugu azilala;
    fundo zake zomwe zamugwetsa.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde
    ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Msampha wamkola mwendo;
    khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Amutchera msampha pansi mobisika;
    atchera diwa pa njira yake.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,
    zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,
    tsoka likumudikira.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;
    miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,
    ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;
    awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Mizu yake ikuwuma pansi
    ndipo nthambi zake zikufota
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;
    sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,
    ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,
    kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;
    anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;
    amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

Mawu a Yobu

19 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti,
    ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Inuyo mwandinyoza kwambiri;
    mwanditsutsa mopanda manyazi.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera,
    cholakwachotu nʼchanga.
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga,
    ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira
    ndipo wandizinga ukonde wake.

“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha;
    ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa;
    waphimba njira zanga ndi mdima.
Iye wandilanda ulemu wanga
    ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu;
    Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Wandikwiyira ndipo
    akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu,
    akonzekera zodzalimbana nane
    ndipo azungulira nyumba yanga.

13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga;
    wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Abale anga andithawa;
    abwenzi anga andiyiwala.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo;
    ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha,
    ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga;
    ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza;
    akandiona amandinyodola.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane;
    iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha;
    ndapulumuka lokumbakumba.

21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni,
    pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu?
    Kodi simunatope nalo thupi langa?

23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa,
    achikhala analembedwa mʼbuku,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo,
    akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo,
    ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka,
    mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye
    ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi.
    Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!

28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji,
    popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Inu muyenera kuopa lupanga;
    pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga;
    zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

Machitidwe a Atumwi 10:1-23

Kenturiyo Korneliyo Ayitana Petro

10 Ku Kaisareya kunali munthu wina dzina lake Korneliyo, mkulu wa asilikali 100 wa gulu la Italiya. Iye ndi banja lake lonse amapembedza ndi kuopa Mulungu. Iye amathandiza osowa mowolowamanja ndipo amapemphera kwa Mulungu nthawi zonse. Tsiku lina, nthawi ili ngati 3 koloko masana, anaona masomphenya. Anaona bwino ndithu mngelo wa Mulungu, amene anabwera kwa iye ndi kuti, “Korneliyo.”

Korneliyo anamuyangʼanitsitsa mngeloyo mwa mantha. Iye anafunsa kuti, “Nʼchiyani kodi Ambuye?”

Mngelo anayankha kuti, “Mapemphero ako ndi zachifundo zako zafika pamaso pa Mulungu ngati chikumbutso. Tsopano tuma anthu apite ku Yopa kuti akayitane munthu dzina lake Simoni Petro. Iye akukhala ndi Simoni mmisiri wa zikopa, amene nyumba yake ili mʼmbali mwa nyanja.”

Mngeloyo anayankhula naye anachoka, Korneliyo anayitana antchito ake awiri ndiponso msilikali mmodzi wa iwo amene ankamutumikira yemwe ankapembedza Mulungu. Iye anawafotokozera zonse zimene zinachitika ndipo anawatuma kuti apite ku Yopa.

Masomphenya a Petro

Mmawa mwake, nthawi ili ngati 12 koloko anthuwo atayandikira mzindawo, Petro anakwera pa denga kukapemphera. 10 Iye anamva njala ndipo anafuna chakudya, ndipo akukonza chakudyacho, iye anachita ngati wakomoka. 11 Iye anaona kuthambo kutatsekuka, ndi chinthu china chikutsitsidwa pansi chooneka ngati chinsalu chachikulu chomangidwa pa msonga zake zinayi. 12 Mʼmenemo munali nyama zonse zamiyendo inayi pamodzinso ndi zokwawa za dziko lapansi ndiponso mbalame zamlengalenga. 13 Petro anamva mawu akuti, “Petro, dzuka, ipha nudye.”

14 Petro anayankha kuti, “Ayi, Ambuye! Ine sindinadyepo kanthu kosayeretsedwa kapena konyansa.”

15 Petro anamvanso kachiwiri mawu akuti, “Usachiyese chonyansa chimene Mulungu wachiyeretsa.”

16 Zimenezi zinachitika katatu ndipo nthawi yomweyo chinsalu chija chinatengedwanso kupita kumwamba.

17 Petro akuganizira za tanthauzo la masomphenyawo, anthu amene Korneliyo anawatuma anapeza kumene kunali nyumba ya Simoni ndipo anayima pa chipata. 18 Iwo anayitana nafunsa ngati Simoni amene amadziwika ndi dzina loti Petro amakhala kumeneko.

19 Petro akuganizirabe za masomphenyawo, Mzimu Woyera anati kwa iye, “Simoni, anthu atatu akukufunafuna. 20 Dzuka, tsika. Usakayike upite nawo pakuti ndawatuma ndine.”

21 Petro anatsika ndipo anati kwa anthuwo, “Amene mukufunayo ndine. Mwabwera kuno chifukwa chiyani?”

22 Anthuwo anayankha kuti, “Ife tachokera kwa Korneliyo, mkulu woyangʼanira asilikali 100. Iye ndi munthu wolungama ndiponso woopa Mulungu, amene amalemekezedwa ndi Ayuda onse. Mngelo woyera anamuwuza kuti mupite ku nyumba yake kuti akamve mawu amene inu mukanene.” 23 Pamenepo Petro anawalowetsa mʼnyumba ndipo anawasamala ngati alendo ake. Mmawa mwake Petro ananyamuka napita nawo ndipo abale ena a ku Yopa anapita naye pamodzi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.