Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yobu 5-7

“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?
    Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Mkwiyo umapha chitsiru,
    ndipo njiru imawononga wopusa.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,
    koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;
    amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake,
    amamutengera ndi za pa minga pomwe,
    ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,
    ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike
    monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.

“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;
    ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
    zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,
    ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Iye amakweza anthu wamba,
    ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,
    kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,
    ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana;
    nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;
    amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,
    ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.

17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;
    nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;
    Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,
    mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,
    ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,
    ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;
    udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,
    ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Udzafika ku manda utakalamba,
    monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.

27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,
    choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

Mawu a Yobu

Tsono Yobu anayankha kuti,

“Achikhala mavuto anga anayezedwa,
    ndipo zipsinjo zanga zonse zikanayikidwa pa sikelo!
Ndithu, zikanalemera kupambana mchenga wa ku nyanja;
    nʼchifukwa chake mawu anga akhala okhadzula.
Mivi ya Wamphamvuzonse yandibaya,
    thupi langa likumva ululu wa miviyo;
    zoopsa za Mulungu zandizinga.
Kodi bulu wakuthengo amalira akakhala ndi msipu,
    nanga ngʼombe imalira ikakhala ndi chakudya?
Kodi chakudya chosakoma nʼkuchidya chopanda mchere,
    nanga choyera cha dzira chimakoma?
Zakudya zimenezi sindifuna nʼkuzilawa komwe;
    zakudya zimenezi zimabwerera kukhosi.

“Aa, ndikanalandira chimene ndikuchipempha,
    chikhala Mulungu anandipatsa chimene ndikuchiyembekezera,
achikhala chinamukomera Mulungu kuti anditswanye,
    kulola dzanja lake kuti lindimenye ndi kundiwonongeratu!
10 Pamenepo ine ndikanakhalabe ndi chitonthozo ichi,
    ndikanakondwa mu ululu wanga wosalekezawu
    podziwa kuti sindinakane mawu a Woyerayo.

11 “Kodi mphamvu zanga nʼzotani kuti ndizikhalabe ndi chiyembekezo?
    Nanga zoyembekezera zanga nʼzotani kuti ndipirirebe?
12 Kodi ine ndili ndi mphamvu?
    Nanga thupi langa ndi lolimba ngati chitsulo?
13 Kodi ndili ndi mphamvu zodzithandizira ndekha,
    nanga pakuti thandizo lachotsedwa kwa ine?

14 “Munthu amene ali kakasi ayenera kukhala ndi abwenzi odzipereka,
    ngakhale kuti iyeyo wasiya kuopa Wamphamvuzonse.
15 Koma abale anga ndi wosadalirika ngati mitsinje yowuma msanga,
    ngati mitsinje imene imathamanga.
16 Ali ngati mitsinje ya madzi akuda nthawi ya dzinja,
    imene madzi ake amakhala ambiri chifukwa chakuchuluka kwa mvula,
17 koma madziwo amasiya kuyenda nthawi yachilimwe,
    ndipo nthawi yotentha madziwo amawumiratu mʼmitsinjemo.
18 Anthu oyenda pa ngamira amapatukirako kufuna madzi;
    iwo amangoyendayenda nʼkufera mʼchipululu.
19 Anthu oyenda pa ngamira a ku Tema amafunafuna madzi,
    anthu amalonda apaulendo a ku Seba amafunafuna mwa chiyembekezo.
20 Amataya mtima chifukwa ankayembekezera kupeza madzi;
    koma akafika kumeneko, amangokhumudwako.
21 Tsono inunso mukuonetsa kuti ndinu osathandiza,
    mukuona chinthu choopsa kwambiri ndipo mukuchita mantha.
22 Kodi ine ndinanenapo kuti, ‘Ndiperekereni kenakake,
    ndilipirireni dipo kuchokera pa chuma chanu,
23 ndilanditseni mʼdzanja la mdani,
    ndiwomboleni mʼdzanja la munthu wankhanza?’

24 “Phunzitseni, ndipo ine ndidzakhala chete;
    ndionetseni pomwe ndalakwitsa.
25 Ndithu, mawu owona ndi opweteka!
    Koma mawu anu otsutsa akufuna kuonetsa chiyani?
26 Kodi inu mukufuna kundidzudzula pa zimene ndikunena,
    ndipo mukufuna kuyesa mawu a munthu wosweka mtima ngati mphepo chabe?
27 Inu mungathe kuchita maere kuti mugulitse ana amasiye
    ndi kumugulitsa bwenzi lanu.

28 “Koma tsopano ndichitireni chifundo pamene mukundiyangʼana.
    Kodi ine ndingayankhule zabodza pamaso panu?
29 Fewani mtima, musachite zosalungama;
    ganiziraninso popeza chilungamo changa chikanalipobe.
30 Kodi pali choyipa chilichonse pa milomo yanga?
    Kodi pakamwa panga sipangathe kuzindikira kanthu koyipa?

“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?
    Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,
    kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,
    ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’
    Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,
    khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,
    ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;
    sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Amene akundiona tsopano akundiona;
    mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,
    momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake
    ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;
    ndidzayankhula mopsinjika mtima,
    ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja
    kuti inu mundiyikire alonda?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga
    ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto
    ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,
    kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.
    Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,
    kuti muzisamala zochita zake,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse
    ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda
    kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,
    Inu wopenyetsetsa anthu?
Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?
    Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga
    ndi kundichotsera machimo anga?
Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;
    mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

Machitidwe a Atumwi 8:1-25

Ndipo Saulo anavomerezana nawo pa imfa ya Stefano.

Kuzunzika kwa Mpingo

Tsiku lomwelo, mpingo wa mu Yerusalemu unayamba kuzunzidwa, ndipo onse, kupatulapo atumwi, anabalalikira ku madera onse a Yudeya ndi Samariya. Anthu okonda Mulungu anayika maliro a Stefano ndipo anamulira kwambiri. Koma Saulo anayamba kuwononga mpingo. Amapita nyumba ndi nyumba, ndipo amagwira amuna ndi amayi ndi kukawatsekera ku ndende.

Filipo ku Samariya

Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita. Filipo anapita ku mzinda wa ku Samariya ndipo analalikira za Khristu kumeneko. Gulu la anthu litamva Filipo akulalikira komanso kuona zizindikiro zozizwitsa zimene ankazichita, onse anamvetsetsa zimene iye amanena. Mizimu yoyipa inatuluka mwa anthu ambiri ikufuwula kwambiri ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo ndi olumala anachiritsidwa. Kotero munali chimwemwe chachikulu mu mzindawo.

Simoni Wamatsenga

Koma mu mzindawo munali munthu dzina lake Simoni, amene amachita za matsenga ndi kudabwitsa anthu a mu Samariya. Iye amadzitamandira kuti ndi wopambana, 10 ndipo anthu onse, aakulu ndi aangʼono anamumvera ndi kunena kuti, “Munthu uyu ndi mphamvu ya Mulungu yotchedwa Mphamvu yayikulu.” 11 Anthu amamutsata chifukwa kwa nthawi yayitali amawadabwitsa ndi matsenga akewo. 12 Koma atakhulupirira Filipo akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ndiponso dzina la Yesu Khristu, anthuwo anabatizidwa amuna ndi amayi. 13 Nayenso Simoni anakhulupirira ndipo anabatizidwa, natsatira Filipo kulikonse, ndipo anadabwa kwambiri pamene anaona zizindikiro zazikulu ndi zozizwitsa.

14 Atumwi a ku Yerusalemu atamva kuti anthu a ku Samariya analandira Mawu a Mulungu, anatumiza Petro ndi Yohane. 15 Atafika anawapempherera kuti alandire Mzimu Woyera, 16 chifukwa Mzimu Woyera anali asanafike pa wina aliyense wa iwo; anali atangobatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu. 17 Ndipo Petro ndi Yohane anasanjika manja awo pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

18 Simoni ataona kuti Mzimu anaperekedwa kwa iwo atumwi atawasanjika manja, iye anafuna kuwapatsa ndalama ndipo anati, 19 “Inenso ndipatseni mphamvu imeneyi kuti aliyense amene ndimusanjika manja anga azilandira Mzimu Woyera.”

20 Petro anayankha kuti, “Ndalama zako utayike nazo pamodzi, chifukwa unaganiza kuti ungathe kugula mphatso ya Mulungu ndi ndalama! 21 Ulibe gawo kapena mbali pa utumikiwu, chifukwa mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu. 22 Lapa zoyipa zakozi ndipo upemphere kwa Ambuye. Mwina adzakukhululukira maganizo a mu mtima mwako. 23 Pakuti ine ndikuona kuti ndiwe wowawidwa mtima ndiponso kapolo wa tchimo.”

24 Ndipo Simoni anayankha, “Mundipempherere kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.”

25 Atatha kuchitira umboni ndi kulalikira mawu a Ambuye, Petro ndi Yohane anabwerera ku Yerusalemu, atalalikira Uthenga Wabwino mʼmidzi yambiri ya Asamariya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.