Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Obadiya

Masomphenya a Obadiya

Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,
“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;
    udzanyozedwa kwambiri.
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
    iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe
    ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,
iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,
    ‘Ndani anganditsitse pansi?’
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga
    ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,
    kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,
aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!
    Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Ngati anthu othyola mphesa akanafika,
    kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,
    chuma chake chobisika chidzabedwa!
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;
    abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;
amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,
    koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,
    kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,
    anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,
    ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau
    adzaphedwa pa nkhondo.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,
    udzakhala wamanyazi;
    adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Pamene adani
    ankamulanda chuma chake
pamene alendo analowa pa zipata zake
    ndi kuchita maere pa Yerusalemu,
    pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako
    pa nthawi ya tsoka lake,
kapena kunyogodola Ayuda
    chifukwa cha chiwonongeko chawo,
kapena kuwaseka pa nthawi ya
    mavuto awo.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga
    pa nthawi ya masautso awo,
kapena kuwanyogodola
    pa tsiku la tsoka lawo,
kapena kulanda chuma chawo
    pa nthawi ya masautso awo.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu
    kuti uphe Ayuda othawa,
kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka
    pa nthawi ya mavuto awo.”

15 “Tsiku la Yehova layandikira
    limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;
    zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera,
    koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;
iwo adzamwa ndi kudzandira
    ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;
    phirilo lidzakhala lopatulika,
ndipo nyumba ya Yakobo
    idzalandira cholowa chake.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto
    ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;
nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,
    ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.
Sipadzakhala anthu opulumuka
    kuchokera mʼnyumba ya Esau.”
            Yehova wayankhula.

19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala
    ku mapiri a Esau,
ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri
    adzatenga dziko la Afilisti.
Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,
    ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo
    adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;
a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi
    adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni
    ndipo adzalamulira mapiri a Esau.
    Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

Chivumbulutso 9

Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi. Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo. Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu. Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.

Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu. Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango. Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo. 10 Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu. 11 Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga).

12 Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.

13 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu. 14 Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.” 15 Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu. 16 Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.

17 Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule. 18 Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo. 19 Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.

20 Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula. 21 Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.