Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Amosi 4-6

Israeli Sanabwerere kwa Mulungu

Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya,
    inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa
    ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti,
    “Nthawi idzafika ndithu
pamene adzakukokani ndi ngowe,
    womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma
    aliyense payekhapayekha,
    ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,”
            akutero Yehova.
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe;
    ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa.
Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse,
    bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko
    ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu.
Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo,
    pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,”
            akutero Ambuye Yehova.

“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse,
    ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu.
    Komatu inu simunabwerere kwa Ine,”
            akutero Yehova.

“Ndinenso amene ndinamanga mvula
    patangotsala miyezi itatu kuti mukolole.
Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina,
    koma pa mzinda wina ayi,
mvula inkagwa pa munda wina;
    koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi,
    koma sanapeze madzi okwanira kumwa.
    Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
            akutero Yehova.

“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa,
    ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu.
Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi.
    Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
            akutero Yehova.

10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu
    monga ndinachitira ku Igupto.
Ndinapha anyamata anu ndi lupanga,
    ndinapereka akavalo anu kwa adani.
Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo.
    Komatu inu simunabwerere kwa Ine,”
            akutero Yehova.

11 “Ndinawononga ena mwa inu
    monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora.
Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto.
    Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
            akutero Yehova.

12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli,
    chifukwa ndidzakuchitira zimenezi,
    konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”

13 Iye amene amawumba mapiri,
    amalenga mphepo,
    ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake,
Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima,
    ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi,
    dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

Mawu Odandawulira Aisraeli

Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:

“Namwali Israeli wagwa,
    moti sadzadzukanso,
wasiyidwa mʼdziko lake lomwe,
    popanda woti ndi kumudzutsa.”

Ambuye Yehova akuti,

“Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu
    udzatsala ndi anthu 100 okha;
mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu
    udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”

Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi:

“Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
    musafunefune Beteli,
musapite ku Giligala,
    musapite ku Beeriseba.
Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,
    ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo,
    mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto;
motowo udzawononga,
    ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.

Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa
    ndi kunyoza chilungamo.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana,
    amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa
    ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku,
amene amayitana madzi a mʼnyanja
    ndi kuwathira pa dziko lapansi,
    Yehova ndiye dzina lake.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu
    ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu
    ndi kunyoza amene amanena zoona.

11 Mumapondereza munthu wosauka
    ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu.
Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema,
    inuyo simudzakhalamo.
Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa,
    inu simudzamwa vinyo wake.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu
    ndi kukula kwa machimo anu.

Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu
    ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu,
    popeza ndi nthawi yoyipa.

14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa,
    kuti mukhale ndi moyo.
Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu,
    monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino;
    mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu.
Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo
    anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.

16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena:

“Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula,
    ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse.
Adzayitana alimi kuti adzalire,
    ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha,
    pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,”
            akutero Yehova.

Tsiku la Yehova

18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka
    tsiku la Yehova!
Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova?
    Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango
    amakumana ndi chimbalangondo,
ngati pamene munthu walowa mʼnyumba,
    natsamira dzanja lake pa khoma
    ndipo njoka nʼkuluma.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala,
    mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?

21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza;
    sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya,
    Ine sindidzazilandira.
Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano,
    Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu!
    Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi,
    chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!

25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja
    munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu,
    ndi nyenyezi ija Kaiwani,
    mulungu wanu,
    mafano amene munadzipangira.
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,”
    akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,
    ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,
inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,
    kumene Aisraeli amafikako!
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;
    mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,
    ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.
Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?
    Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,
    zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,
    mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.
Mumadya ana ankhosa onona
    ndi ana angʼombe onenepa.
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka
    nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza
    ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,
    koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;
    maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,
    ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;
Ine ndidzawupereka mzindawu
    pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11 Pakuti Yehova walamula kuti
    nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,
    ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?
    Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?
Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha
    ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara
    ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,
    “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu
umene udzakuzunzani
    kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

Chivumbulutso 7

Anthu 144,000

Zitatha izi ndinaona angelo anayi atayima pa mbali zinayi za dziko lapansi, atagwira mphepo zinayi za dziko lapansi kuletsa kuti mphepo iliyonse isawombe pa dziko kapena pa nyanja kapena pa mtengo uliwonse. Kenaka ndinaona mngelo wina akuchokera kummawa, ali ndi chidindo cha Mulungu wamoyo. Iye anafuwulira angelo anayi aja amene anapatsidwa mphamvu yowononga dziko ndi nyanja kuti, “Musawononge dziko, nyanja ndi mitengo kufikira titalemba chizindikiro pa mphumi za atumiki a Mulungu wathu.” Choncho ndinamva chiwerengero cha amene ankayenera kulembedwa chizindikiro aja. Analipo okwanira 144,000 kuchokera ku mafuko onse a Israeli.

Ochokera fuko la Yuda analipo 12,000 amene analembedwa chizindikiro.

Ochokera fuko la Rubeni analipo 12,000;

ochokera fuko la Gadi analipo 12,000;

ochokera fuko la Aseri analipo 12,000;

ochokera fuko la Nafutali analipo 12,000;

ochokera fuko la Manase analipo 12,000;

ochokera fuko la Simeoni analipo 12,000;

ochokera fuko la Levi analipo 12,000;

ochokera fuko la Isakara analipo 12,000;

ochokera fuko la Zebuloni analipo 12,000;

ochokera fuko la Yosefe analipo 12,000;

ochokera fuko la Benjamini analipo 12,000.

Gulu Lalikulu la Anthu Ovala Zoyera

Zitatha izi ndinayangʼana patsogolo panga ndipo ndinaona gulu lalikulu la anthu loti munthu sangathe kuliwerenga lochokera dziko lililonse, fuko lililonse, mtundu wa anthu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse, atayima patsogolo pa mpando waufumu, pamaso pa Mwana Wankhosa. Iwo anali atavala mikanjo yoyera ndi kunyamula nthambi za kanjedza mʼmanja mwawo. 10 Ndipo ankafuwula mokweza kuti:

“Chipulumutso chimachokera kwa Mulungu wathu,
wokhala pa mpando waufumu
ndi kwa Mwana Wankhosa.”

11 “Angelo onse anayimirira kuzungulira mpando waufumu uja, kuzunguliranso akuluakulu aja ndi zamoyo zinayi zija. Angelo aja anadzigwetsa pansi chafufumimba patsogolo pa mpando waufumu napembedza Mulungu. 12 Iwo anati,

“Ameni!
Matamando ndi ulemerero,
nzeru, mayamiko, ulemu,
ulamuliro ndi mphamvu
zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi,
Ameni!”

13 Pamenepo mmodzi wa akuluakulu aja anandifunsa kuti, “Kodi avala mikanjo yoyerawa ndani ndipo akuchokera kuti?”

14 Ine ndinayankha kuti, “Mbuye wanga mukudziwa ndinu.”

Tsono iye anandiwuza kuti, “Amenewa ndi amene anatuluka mʼmazunzo aakulu aja. Anachapa mikanjo yawo naziyeretsa mʼmagazi a Mwana Wankhosa. 15 Nʼchifukwa chake,

“iwowa ali patsogolo pa mpando waufumu wa Mulungu
    ndipo akutumikira usana ndi usiku mʼNyumba ya Mulungu;
ndipo Iye wokhala pa mpando waufumu
    adzawaphimba ndi tenti yake.
16 ‘Iwowa sadzamvanso njala,
    sadzamvanso ludzu,
dzuwa kapena kutentha kulikonse
    sikudzawawotcha.’
17 Pakuti Mwana Wankhosa amene ali pakati pa mpando waufumu
    adzakhala mʼbusa wawo.
‘Iye adzawatsogolera ku akasupe a madzi amoyo.’
    ‘Ndipo Mulungu adzawapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.