Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Hoseya 12-14

12 Efereimu amadya mpweya;
    tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa
    ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.
Amachita mgwirizano ndi Asiriya
    ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Yehova akuyimba mlandu Yuda;
    Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,
    adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;
    iye atakula analimbana ndi Mulungu.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;
    analira napempha kuti amukomere mtima.
Mulungu anakumana naye ku Beteli
    ndipo anayankhula naye kumeneko,
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
    Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;
    pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,
    ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;
    iyeyo amakonda kubera anthu.
Efereimu amadzitama ponena kuti,
    “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.
Palibe amene angandiloze chala
    chifukwa cha kulemera kwanga.”

“Ine ndine Yehova Mulungu wako
    amene ndinakutulutsa mu Igupto.
Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,
    monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Ndinayankhula ndi aneneri,
    ndinawaonetsa masomphenya ambiri,
    ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11 Kodi Giliyadi ndi woyipa?
    Anthu ake ndi achabechabe!
Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?
    Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala
    mʼmunda molimidwa.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,
    Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,
    ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;
    kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.
    Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.
    Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

13 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;
    anali wolemekezeka mu Israeli.
    Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;
    akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,
zifanizo zopangidwa mwaluso,
    zonsezo zopangidwa ndi amisiri.
Amanena za anthu awa kuti,
    “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe
    ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,
    ngati mame amene amakamuka msanga,
    ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,
    ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndinakutulutsani mu Igupto.
Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,
    palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
Ndinakusamalira mʼchipululu,
    mʼdziko lotentha kwambiri.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;
    iwo atakhuta anayamba kunyada;
    ndipo anandiyiwala Ine.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango,
    ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,
    ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.
Ndidzawapwepweta ngati mkango;
    chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

“Iwe Israeli, wawonongedwa,
    chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?
    Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,
amene iwe unanena za iwo kuti,
    ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,
    ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,
    machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,
    koma iye ndi mwana wopanda nzeru,
pamene nthawi yake yobadwa yafika
    iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;
    ndidzawawombola ku imfa.
Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?
    Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,
15     ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,
mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,
    ikuwomba kuchokera ku chipululu.
Kasupe wake adzaphwa
    ndipo chitsime chake chidzawuma.
Chuma chake chonse chamtengowapatali
    chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,
    chifukwa anawukira Mulungu wawo.
Adzaphedwa ndi lupanga;
    ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,
    akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

Kulapa Kubweretsa Madalitso

14 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.
    Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Bweretsani zopempha zanu
    ndipo bwererani kwa Yehova.
Munene kwa Iye kuti,
    “Tikhululukireni machimo athu onse
ndi kutilandira mokoma mtima,
    kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Asiriya sangatipulumutse;
    ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,
sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’
    kwa zimene manja athu omwe anazipanga,
    pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”

Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo
    ndipo ndidzawakonda mwaufulu
    pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli
    Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.
Adzazika mizu yake pansi
    ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
    mphukira zake zidzakula.
Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,
    kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.
    Iye adzakula bwino ngati tirigu.
Adzachita maluwa ngati mphesa
    ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?
    Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.
Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;
    zipatso zako zimachokera kwa Ine.”

Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.
    Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.
Njira za Yehova ndi zolungama;
    anthu olungama amayenda mʼmenemo,
    koma anthu owukira amapunthwamo.

Chivumbulutso 4

Mapembedzedwe a Kumpando Waufumu Kumwamba

Kenaka, nditayangʼana patsogolo panga ndinaona khomo lotsekuka la kumwamba. Ndipo liwu lija ndinalimva poyamba lokhala ngati lipenga linati, “Bwera kuno, ndipo ndidzakuonetsa zimene zichitike zikatha izi.” Nthawi yomweyo ndinatengedwa ndi Mzimu Woyera, ndipo patsogolo panga ndinaona mpando waufumu wina atakhalapo. Ndipo amene anakhalapoyo anali wa maonekedwe ngati miyala ya jasipa ndi sardiyo. Utawaleza wooneka ngati simaragido unazinga mpando waufumuwo. Kuzungulira mpando waufumuwu panalinso mipando ina yaufumu yokwana 24 ndipo panakhala akuluakulu 24 atavala zoyera ndipo anavala zipewa zaufumu zagolide pamutu. Kumpando waufumuwo kunkatuluka mphenzi, phokoso ndi mabingu. Patsogolo pake pa mpando waufumuwo panali nyale zisanu ndi ziwiri zoyaka. Iyi ndiyo mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu. Patsogolo pa mpando waufumu pomwepo panalinso ngati nyanja yagalasi yonyezimira ngati mwala wa krustalo.

Pakatinʼpakati, kuzungulira mpando waufumuwo panali zamoyo zinayi zokhala ndi maso ponseponse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe. Chamoyo choyamba chinali ngati mkango, chachiwiri chinali ngati mwana wangʼombe, chachitatu chinali ndi nkhope ngati munthu, chachinayi chinali ngati chiwombankhanga chowuluka. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko asanu ndi limodzi, ndipo chinali ndi maso ponseponse ndi mʼkati mwa mapiko momwe. Usana ndi usiku zimanena mosalekeza kuti,

“Woyera, woyera, woyera
ndi Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,
amene munali, amene muli ndi amene mukubwera.”

Nthawi zonse zamoyozo zimapereka ulemerero, ulemu ndi mayamiko kwa uja wokhala pa mpando waufumu, amene ali ndi moyo wamuyaya. 10 Izi zikamachitika akuluakulu 24 aja amadzigwetsa pansi pamaso pa wokhala pa mpando waufumuyo, namupembedza wokhala ndi moyo wamuyayayo. Iwo amaponya pansi zipewa zawo zaufumu patsogolo pa mpando waufumu nati:

11 “Ndinu woyeneradi kulandira ulemerero ndi ulemu ndi mphamvu,
    Ambuye ndi Mulungu wathu,
pakuti munalenga zinthu zonse,
    ndipo mwakufuna kwanu
    zinalengedwa monga zilili.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.