Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yeremiya 48-49

Uthenga Wonena za Mowabu

48 Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.
    Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;
    linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Palibenso amene akutamanda Mowabu;
    ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:
    ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’
Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;
    ankhondo adzakupirikitsani.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.
    Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Mowabu wawonongeka;
    ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,
    akulira kwambiri pamene akupita.
Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka
    pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Thawani! Dzipulumutseni;
    khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,
    nanunso mudzatengedwa ukapolo,
ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,
    pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,
    ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.
Chigwa chidzasanduka bwinja
    ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa
    monga Yehova wayankhulira.
Mtsineni khutu Mowabu
    chifukwa adzasakazika;
mizinda yake idzasanduka mabwinja,
    wopanda munthu wokhalamo.

10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!
    Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,
    ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,
osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;
    iye sanatengedwepo ukapolo.
Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja
    ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”
    akutero Yehova,
“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko
    ndipo adzamukhutula;
adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake
    pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,
    monga momwe Aisraeli anachitira manyazi
    ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.
    Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;
    anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”
    ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;
    masautso ake akubwera posachedwa.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,
    inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;
nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,
    taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18 “Tsikani pa ulemerero wanu
    ndipo khalani pansi powuma,
    inu anthu okhala ku Diboni,
pakuti wowononga Mowabu
    wabwera kudzamenyana nanu,
    wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri,
    imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.
Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,
    afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.
    Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!
Lengezani ku mtsinje wa Arinoni
    kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,
    ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22     Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23     Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24     Keriyoti ndi Bozira
    ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka;
    mkono wake wathyoka,”
            akutero Yehova.

26 “Muledzeretseni Mowabu,
    chifukwa anadzikuza powukira Yehova.
Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;
    mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?
    Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba
kuti nthawi zonse poyankhula za iye,
    iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu,
    siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.
Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake
    pa khomo la phanga.

29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu,
    kunyada kwake nʼkwakukulu.
Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.
    Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake,
            akutero Yehova.
    Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,
    ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,
    ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.
    Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa
imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;
    zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.
Wowononga wasakaza
    zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha
    ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.
Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;
    palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.
Ngakhale kufuwula kulipo,
    koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira
    ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,
kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.
    Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu
    kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera
    ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”
            akutero Yehova.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.
    Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro
    chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Aliyense wameta mutu wake
    ndi ndevu zake;
manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,
    ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu
    ndiponso mʼmisewu yake
anthu akungolira,
    pakuti ndaphwanya Mowabu
    ngati mtsuko wopanda ntchito,”
            akutero Yehova.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!
    Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.
Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,
    chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40 Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga
    chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Mizinda idzagwidwa
    ndipo malinga adzalandidwa.
Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu
    idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu
    chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira
    inu anthu a ku Mowabu,”
            akutero Yehova.
44 “Aliyense wothawa zoopsa
    adzagwera mʼdzenje,
aliyense wotuluka mʼdzenje
    adzakodwa mu msampha.
Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu
    pa nthawi ya chilango chake,”
            akutero Yehova.

45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni
    chifukwa chotopa.
Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,
    malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.
Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,
    dziko la anthu onyada.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu!
    Anthu opembedza Kemosi awonongeka.
Ana ako aamuna ndi aakazi
    atengedwa ukapolo.

47 “Komabe masiku akutsogolo
    ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”
            akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

Uthenga Wonena za Aamoni

49 Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?
    Kapena alibe mlowamʼmalo?
Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?
    Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Koma nthawi ikubwera,”
    akutero Yehova,
“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo
    ku Raba, likulu la Amoni;
ndipo malo awo opembedzera milungu yawo
    adzatenthedwa ndi moto.
Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo
    kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”
            akutero Yehova.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!
    Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!
Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;
    thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,
chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,
    pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Chifukwa chiyani mukunyadira
    chigwa chanu,
inu anthu osakhulupirika
    amene munadalira chuma chanu nʼkumati:
    ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe
    zochokera kwa onse amene akuzungulira,”
            akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.
“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.
    Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”
            akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?
    Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?
    Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Inu anthu a ku Dedani, thawani,
    bwererani ndi kukabisala ku makwalala
chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau
    popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu
    akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Anthu akuba akanafika usiku
    akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.
    Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,
    kotero kuti sadzathanso kubisala.
Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.
    Palibe wonena kuti,
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.
    Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,
“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!
    Konzekerani nkhondo!”

15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.
    Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga;
    kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
iwe amene umakhala mʼmapanga
    a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.
Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.
    Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo
    chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,
    pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”
            akutero Yehova,
“motero palibe munthu
    amene adzakhala mu Edomu.

19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani
    kupita ku malo a msipu wobiriwira,
Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.
    Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.
Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?
    Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova
    ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.
Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo
    ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;
    kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka
    nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu
    idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha
    chifukwa amva nkhani yoyipa.
Mitima yawo yagwidwa ndi mantha
    ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka.
    Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa
    chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.
Ali ndi nkhawa komanso mantha
    ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Mzinda wotchuka
    ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;
    ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”
            akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko;
    moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.
    Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,
    ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.
    Mutengenso ngamira zawo.
Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,
    ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30 “Thawani mofulumira!
    Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”
            akutero Yehova.
“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;
    wakonzekera zoti alimbane nanu.

31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,
    umene ukukhala mosatekeseka,”
            akutero Yehova,
“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;
    anthu ake amakhala pa okha.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa,
    ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.
Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.
    Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”
            akutero Yehova.
33 “Hazori adzasanduka bwinja,
    malo okhalamo nkhandwe
mpaka muyaya.
    Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35 Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,
    umene uli chida chawo champhamvu.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu
    kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;
ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,
    ndipo sipadzakhala dziko
    limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo
    komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.
Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga
    ndipo adzakhala pa mavuto,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga
    mpaka nditawatheratu.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu
    ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”
            akutero Yehova.

39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera
    anthu a ku Elamu dziko lawo,”
            akutero Yehova.

Ahebri 7

Za Melikizedeki Mkulu wa Ansembe

Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa. Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.” Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.

Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha. Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu. Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu. Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo. Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo. Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu, 10 chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.

Yesu Wofanana ndi Melikizedeki

11 Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni? 12 Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha. 13 Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe. 14 Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe. 15 Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki. 16 Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha. 17 Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti,

“Iwe ndi wansembe wamuyaya,
    monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.”

18 Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu. 19 Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.

20 Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro. 21 Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati,

“Ambuye analumbira
    ndipo sangasinthe maganizo ake,
‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’ ”

22 Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.

23 Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi. 24 Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. 25 Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.

26 Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku. 27 Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha. 28 Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.