Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yeremiya 46-47

46 Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.

Uthenga Wonena za Igupto

Kunena za Igupto:

Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,

anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo,
    ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
Mangani akavalo,
    ndipo kwerani inu okwerapo!
Khalani pa mzere
    mutavala zipewa!
Nolani mikondo yanu,
    valani malaya anu ankhondo!
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani?
    Achita mantha
akubwerera,
    ankhondo awo agonjetsedwa.
Akuthawa mofulumirapo
    osayangʼananso mʼmbuyo,
    ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,”
            akutero Yehova.
Waliwiro sangathe kuthawa
    ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka.
Akunka napunthwa ndi kugwa
    kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.

“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo,
    ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
Igupto akusefukira ngati Nailo,
    ngati mitsinje ya madzi amkokomo.
Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi;
    ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
Tiyeni, inu akavalo!
    Thamangani inu magaleta!
Tulukani, inu ankhondo,
    ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango,
    ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse;
    tsiku lolipsira, lolipsira adani ake.
Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi,
    lidzaledzera ndi magazi.
Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe
    mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.

11 “Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala
    iwe namwali Igupto.
Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira;
    palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako;
    kulira kwako kwadzaza dziko lapansi.
Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana,
    onse awiri agwa pansi limodzi.”

13 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:

14 “Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli.
    Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi.
Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza,
    chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa?
    Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa.
    Aliyense akuwuza mnzake kuti,
‘Tiyeni tibwerere kwathu,
    ku dziko kumene tinabadwira,
    tithawe lupanga la adani athu.’
17 Kumeneku iwo adzafuwula kuti,
    ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti,
    Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’

18 “Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu,
    imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse,
“wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena,
    ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo
    inu anthu a ku Igupto,
pakuti Mefisi adzasanduka chipululu
    ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.

20 “Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola,
    koma chimphanga chikubwera
    kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye
    ali ngati ana angʼombe onenepa.
Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi.
    Palibe amene wachirimika.
Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira;
    ndiyo nthawi yowalanga.
22 Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa
    pamene adani abwera ndi zida zawo,
abwera ndi nkhwangwa
    ngati anthu odula mitengo.
23 Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,”
            akutero Yehova,
    “ngakhale kuti ndi yowirira.
Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe,
    moti sangatheke kuwerengeka.
24 Anthu a ku Igupto achita manyazi
    atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”

25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira. 26 Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.

27 “Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha;
    usataye mtima, iwe Israeli.
Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali,
    ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo.
Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere,
    ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha,
    pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova.
“Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu
    a ku mayiko kumene ndakupirikitsira,
    Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu.
Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera;
    sindidzakulekerera osakulanga.”

Uthenga Wonena za Afilisti

47 Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;
    adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.
Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,
    mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.
Anthu adzafuwula;
    anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,
    phokoso la magaleta ake
    ndi kulira kwa mikombero yake.
Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;
    manja awo adzangoti khoba.
Pakuti tsiku lafika
    lowononga Afilisti onse
ndi kupha onse otsala,
    onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.
Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,
    otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
Anthu a ku Gaza ameta mipala;
    anthu a ku Asikeloni akhala chete.
Inu otsala a ku chigwa,
    mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,
    kodi udzapumula liti?
Bwerera mʼmalo ako;
    ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
Koma lupangalo lidzapumula bwanji
    pamene Yehova walilamulira
kuti lithire nkhondo
    Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

Ahebri 6

Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu, za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.

Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera. Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.

Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa. Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.

Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso. 10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano. 11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera. 12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.

Kukhazikika kwa Malonjezo a Mulungu

13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti, 14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.” 15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.

16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse. 17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro. 18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira. 19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga. 20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.